< Sakaria 14 >
1 Så Herrans dag kommer, att du skall varda ett rof och byte.
Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
2 Ty jag skall församla allahanda Hedningar emot Jerusalem till strid; och staden skall varda vunnen, husen skinnad, och qvinnor skämda; hälften af stadenom skall fången bortföras, och det öfverblefna folket skall icke utu stadenom drifvet varda.
Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
3 Men Herren skall draga ut, och strida emot de samma Hedningar, såsom han plägar att strida i stridstid.
Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
4 Ock hans fötter skola på den tiden stå på Oljobergena, som för Jerusalem ligger, östantill; och Oljoberget skall klofna midt i tu stycker, ifrån öster allt intill vester, ganska vidt ifrå hvartannat; så att den ena hälften af bergena skall gifva sig norrut, och den andra söderut.
Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
5 Och I skolen fly ror denna dalenom emellan min berg; ty den dalen emellan bergen skall räcka intill Azal; och skolen fly, lika som I uti förtiden flydden för jordbäfningene i Ussia, Juda Konungs, tid. Så skall Herren, min Gud, komma, och alle helige med dig.
Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
6 På den tiden skall intet ljus vara, utan köld och frost.
Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
7 Och en dag skall varda, den Herranom kunnig är, hvarken dag eller natt, och om aftonen skall det ljust blifva.
Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
8 På den tiden skola rinnande vatten flyta utaf Jerusalem; hälften bortåt hafvet österut, och den andra hälften bortåt det yttersta hafvet; och det skall vara både vinter och sommar.
Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
9 Och Herren skall vara en Konung öfver all land; på den tiden skall Herren vara en, och hans Namn ett.
Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
10 Och man skall gå i allo landena, lika som på en slättmark, ifrå Gibea intill Rimmon, söderut, till Jerusalem; ty han skall upphöjd och besutten varda i sitt rum, ifrå, BenJamins port, intill första portens rum, allt intill hörneporten; och ifrå Hananeels torn, intill Konungens press.
Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
11 Och man skall bo derinne, och ingen spillgifning skall mer vara; ty Jerusalem skall ganska säkert bo.
Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
12 Och detta skall vara plågan, der Herren all folk med plåga skall, som emot Jerusalem stridt hafva; deras kött skall förtvina; medan de ännu stå på deras fötter; och deras ögon förgås uti sin hål, och deras tunga förfaras i deras mun.
Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
13 På den tiden skall Herren låta komma ett stort buller ibland dem, att den ene skall fatta den andra vid handena, och lägga sina hand uppå dens andras hand.
Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
14 Ty ock Juda skall strida emot Jerusalem; på det församlas skola alla de Hedningars gods, som deromkring äro; guld, silfver och kläder, öfvermåtton mycket.
Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
15 Och så skall då denna plågan gå öfver hästar, mular, camelar, åsnar, och allahanda djur, som i härenom äro, såsom denna plågan är.
Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
16 Och alle öfverblefne ibland alla Hedningar, som emot Jerusalem drogo, skola årliga komma upp, till att tillbedja Konungen, Herran Zebaoth, och till att hålla löfhyddohögtid.
Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
17 Men hvad som helst slägte på jordene icke kommer hitupp till Jerusalem, till att tillbedja Konungen, Herran Zebaoth, öfver dem skall intet regn komma.
Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
18 Och om de Egyptiers slägte icke uppfara, och komma, så skall öfver dem ock intet regna. Det skall vara plågan, der Herren alla Hedningar med plåga skall, som icke uppkomma till att hålla löfhyddohögtid.
Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
19 Ty det skall vara de Egyptiers, och alla Hedningars synd, som icke uppkomma till att hålla löfhyddohögtid.
Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
20 På den tiden skall hästarnas rustning vara Herranom helig; och kettlarne i Herrans hus skola vara lika som de skålar för altaret.
Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
21 Ty alle kettlar, både i Jerusalem och Juda, skola Herranom Zebaoth helige vara; så att alle de, som offra vilja, skola komma och taga dem, och koka deruti; och ingen Cananeisk skall mer vara uti Herrans Zebaoths hus, på den tiden.
Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.