< Sakaria 12 >

1 Detta är Herrans ords tunge öfver Israel, säger Herren, den der utsträcker himmelen, och grundar jordena, och menniskones anda gör uti honom:
Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
2 Si, jag vill göra Jerusalem till en fallskål allom folkom deromkring; ty det varder ock Juda gällandes, när Jerusalem belagt varder.
“Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
3 Likväl vill jag på den tiden göra Jerusalem till en tung sten allom folk om; alle de som vilja borthäfva honom, de skola förslita sig på honom; ty alle Hedningar på jordene skola församla sig emot honom.
Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
4 På den tiden, säger Herren, skall jag göra hvar och en häst sky, och hans åsittare ursinnigan; men öfver Juda hus vill jag hafva min ögon öppne, och plåga alla folks hästar med blindhet.
Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
5 Och Förstarna i Juda skola säga uti sitt hjerta: Låt de borgare i Jerusalem hafva ett godt mod i Herranom Zebaoth, deras Gud.
Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
6 På den tiden skall jag göra Juda Förstar till en brinnande ugn i ved, och såsom en eldbrand i halm; så att de skola uppfräta, både på högra sidone och den venstra, all folk omkring sig; och Jerusalem skall åter besuttet varda i sitt rum, i Jerusalem.
“Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
7 Och Herren skall hjelpa Juda hyddor, såsom i förtiden; på det Davids hus icke skall högt berömma sig, eller borgarena i Jerusalem emot Juda.
“Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
8 På den tiden skall Herren beskärma borgarena i Jerusalem; och det skall ske, att den der svag är på den tiden, han skall vara såsom David; och Davids hus skall vara såsom Guds hus, såsom Herrans Ängel för dem.
Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
9 Och på den tiden skall jag tänka till att nederlägga alla Hedningar, som emot Jerusalem dragne äro.
Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
10 Men öfver Davids hus, och öfver borgarena i Jerusalem, skall jag utgjuta nåds och böns Anda; ty de skola se uppå mig, den de genomstungit hafva; och skola begråta honom, lika som man ett enda barn begråter; och skola bedröfva sig om honom, såsom man bedröfvar sig om ett första barn.
“Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
11 På den tiden skall stor klagogråt vara i Jerusalem, lika som det var men HadadRimmon, uti den markene Megiddon.
Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
12 Och landet skall jämra sig, hvart och ett slägte besynnerliga; Davids hus slägte besynnerliga, och deras hustrur besynnerliga; Nathans hus slägte besynnerliga, och deras hustrur besynnerliga;
Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
13 Levi hus slägte besynnerliga, och deras hustrur besynnerliga; Simei hus slägte besynnerliga, och deras hustrur besynnerliga;
nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
14 Alltså alla andras slägter, hvart och ett besynnerliga, och deras hustrur också besynnerliga.
ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.

< Sakaria 12 >