< Höga Visan 6 >

1 Hvart är då din vän gången, o du dägeligasta ibland qvinnor? Hvart hafver din vän vändt sig, så vilje vi honom söka med dig.
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti? Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
2 Min vän är nedergången uti sin örtagård, till örtasängarna, att han sig der förlusta skall i örtagårdarna, och hemta roser.
Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake, ku timinda ta zokometsera zakudya, akukadyetsa ziweto zake ku minda, ndiponso akuthyola maluwa okongola.
3 Min vän är min, och jag är hans, den sig ibland roser förlustar.
Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga; amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
4 Du äst dägelig, min kära, såsom Thirza; lustig såsom Jerusalem, förskräckelig såsom en härordan.
Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
5 Vänd din ögon ifrå mig, förty de göra mig brinnande; ditt hår är såsom en getahjord, de som på berget Gilead klippte äro.
Usandipenyetsetse; pakuti maso ako amanditenga mtima. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
6 Dine tänder äro såsom en fårahjord, de der tvagne komma utu vatten, hvilke allesammans äro med tvillingar hafvande, och ingen ibland dem är ofruktsam.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa, iliyonse ili ndi ana amapasa, palibe imene ili yokha.
7 Dine kinder äro såsom skörden på granatäplet, emellan dina lockar.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu, masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
8 Sextio äro Drottningarna, och åttatio frillorna, och på jungfrurna är intet tal;
Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60, ndi azikazi 80, ndi anamwali osawerengeka;
9 Men en är min dufva, min fromma; en är sine moder kärast, och sine moders utkorada. Då döttrarna sågo henne, prisade de henne saliga; Drottningarna och frillorna lofvade henne.
koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense; mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake, mwana wapamtima wa amene anamubereka. Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala; akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
10 Ho är denna, som uppgår såsom en morgonrodne, dägelig såsom månen, utkorad såsom solen, förskräckelig såsom en härordan?
Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha, wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa, wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
11 Jag är nedergången i nöttagården, till att skåda telningarna vid bäcken; till att skåda, om vinträt blomstrades, om granatäplen grönskades.
Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa, kukaona ngati mpesa waphukira kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Min själ visste icke, att han mig intill AmmiNadibs vagnar satt hade.
Ndisanazindikire kanthu, ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
13 Vänd om, vänd om, o Sulamith; vänd om, vänd om, att vi måge skåda dig; hvad sen I på Sulamith annat, än dans i Mahanaim?
Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami; bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe! Mwamuna Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami, pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

< Höga Visan 6 >