< Psaltaren 99 >
1 Herren är Konung, derföre vredgas folken; han sitter på Cherubim, derföre upprörer sig verlden.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Herren är stor i Zion, och hög öfver all folk.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Man tacke ditt stora och underliga Namn, det heligt är.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 Uti denna Konungens rike älskar man det rätt är; du gifver fromhet, du skaffar dom och rättfärdighet i Jacob.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Upphöjer Herran vår Gud; tillbedjer vid hans fotapall; ty han är helig.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Mose och Aaron ibland hans Prester, och Samuel ibland dem som hans Namn åkalla; de åkallade Herran, och han bönhörde dem.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 Han talade med dem genom en molnstod; de höllo hans vittnesbörd och bud, som han dem gaf.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 Herre, du äst vår Gud; du bönhörde dem; du, Gud, gaf dem till, och straffade deras verk.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Upphöjer Herran vår Gud, och tillbedjer på hans helga berg; tv Herren vår Gud är helig.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.