< Psaltaren 98 >
1 En Psalm. Sjunger Herranom en ny viso, ty han gör underlig ting; han vinner seger med sine högra hand, och med sinom helga arm.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 Herren låter förkunna sina salighet; för folken låter han uppenbara sina rättfärdighet.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 Han tänker uppå sina nåde och sanning Israels huse; alle verldenes ändar se vår Guds salighet.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Glädjens Herranom, all verlden; sjunger, priser och lofver.
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Lofver Herran med harpor, med harpor och psalmer;
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 Med trummeter och basuner; fröjdens för Herranom, Konungenom.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Hafvet fräse, och hvad deruti är; jordenes krets, och de deruppå bo.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Vattuströmmarna fröjde sig, och all berg vare glad,
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 För Herranom; ty han kommer till att döma jordena; han skall döma jordenes krets med rättfärdighet, och folken med rätt.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.