< Psaltaren 96 >
1 Sjunger Herranom en ny viso; sjunger Herranom all verlden.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Sjunger Herranom, och lofver hans Namn; prediker den ena dagen efter den andra hans salighet.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Förtäljer ibland Hedningarna hans äro, ibland all folk hans under.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Ty Herren är stor, och högt prisandes; underlig öfver alla gudar.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Ty alle folkens gudar äro afgudar; men Herren hafver gjort himmelen.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Det står härliga och kosteliga till för honom, och går väldeliga och lofliga till i hans helgedom.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 I folk, bärer fram Herranom; bärer fram Herranom äro och magt.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Bärer fram Herranom hans Namns äro; bärer skänker, och kommer i hans gårdar.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Tillbedjer Herran i heligo prydning; hela verlden frukte honom.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Säger ibland Hedningarna, att Herren är Konung, och hafver sitt rike, så vidt som verlden är, beredt, att det blifva skall; och dömer folken rätt.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Himmelen fröjde sig, och jorden vare glad. hafvet fräse, och hvad deruti är.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Marken vare glad, och allt det derpå är, och låter all trä i skogen fröjda sig,
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 För Herranom; ty han kommer; ty han kommer till att döma jordena; han skall döma jordenes krets med rättfärdighet, och folken med sine sanning.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.