< Psaltaren 94 >

1 Herre Gud, hvilkom hämnden tillhörer; Gud, hvilkom hämnden tillhörer, bete dig.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Upphöj dig, du verldenes domare; vedergäll dem högfärdigom det de förtjena.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Herre, huru länge skola de ogudaktige, huru länge skola de ogudaktige pråla;
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Och så högmodeliga tala; och alle ogerningsmän så berömma sig?
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Herre, de förtrycka ditt folk, och plåga ditt arf.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Enkor och främlingar dräpa de, och faderlösa döda de;
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Och säga: Herren ser det intet; och Jacobs Gud aktar det intet.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Märker dock, I galne ibland folket; och I dårar, när viljen I vise varda?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Den der örat planterat hafver, skulle han icke höra? Den der ögat gjort hafver, skulle han icke se?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Den der Hedningarna näpser, skulle han icke straffa? den der menniskorna lärer hvad de veta.
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Men Herren vet menniskornas tankar, att de fåfängelige äro.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Säll är den som du, Herre, tuktar, och lärer honom genom din lag;
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 Att han tålamod hafva må, då illa går; tilldess dem ogudaktiga grafven beredd varder.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Ty Herren skall icke förkasta sitt folk, eller öfvergifva sitt arf.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Ty rätt måste dock blifva rätt; och thy måste all from hjerta tillfalla.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Ho står med mig emot de onda? Ho träder till mig emot de ogerningsmän?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Om Herren icke hulpe mig, så låge min själ fulltnär uti det stilla.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Jag sade: Min fot hafver stapplat; men din nåd, Herre, uppehöll mig.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Jag hade mycket bekymmer i mitt hjerta; men din tröst gladde mina själ.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Du kommer ju aldrig öfverens med dem skadeliga stolenom, som lagen illa uttyder.
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 De rusta sig emot dens rättfärdigas själ, och fördöma oskyldigt blod.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Men Herren är mitt beskärm, min Gud är mitt hopps tröst.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Och han skall vedergälla dem deras orätt, och skall förgöra dem för deras ondskos skull; Herren, vår Gud, skall förgöra dem.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psaltaren 94 >