< Psaltaren 75 >

1 En Psalm och visa Assaphs, att han icke förgicks, till att föresjunga. Vi tacke dig, Gud, vi tacke dig, och förkunne din under, att ditt Namn så när är.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Ty i sinom tid skall jag rätt döma.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 Jorden bäfvar, och alle de derpå bo; men jag håller hennes pelare stadiga. (Sela)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Jag sade till de stortaliga: Berömmer eder icke så; och till de ogudaktiga: Trugens icke uppå välde;
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Trugens icke så fast uppå edart välde; taler icke så halsstyft.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Det hafver ingen nöd hvarken af östan eller vestan, eller af de berg i öknene.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Ty Gud är domare; denna förnedrar han, och den andra upphöjer han.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Ty Herren hafver en skål i handene, och med starkt vin fullt inskänkt, och skänker derutaf; men de ogudaktige måste alle dricka, och utsupa dräggena.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Men jag vill förkunna evinnerliga, och lofsjunga Jacobs Gudi;
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Och vill sönderbryta allt de ogudaktigas våld; att de rättfärdigas välde skall upphöjdt varda.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psaltaren 75 >