< Psaltaren 64 >

1 En Psalm Davids, till att föresjunga. Hör, Gud, mina röst, i mine klagan. Bevara mitt lif för den grufveliga fiendan.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Förskyl mig för de ondas församling; för deras hop, som illa göra;
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 De der skärpa sina tungor, såsom ett svärd, och skjuta med sina förgiftiga ord, såsom med pilar;
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Att de måga lönliga skjuta den fromma; med hast skjuta de uppå honom, utan all fruktan.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 De äro djerfve med sin onda anslag, och talas vid, huru de snaror lägga vilja, och säga: Ho kan se dem?
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 De dikta skalkhet, och hållat hemliga; de äro illfundige, och hafva listig skalkastycke före.
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Men Gud skall hasteliga skjuta dem, så att dem skall svida efter.
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 Deras egen tunga skall fälla dem; så att dem bespotta skall hvar och en, som dem ser.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 Och alla menniskor, som det se, skola frukta sig, och säga: Det hafver Gud gjort; och förmärka, att det är hans gerning.
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 De rättfärdige skola fröjda sig af Herranom, och förtrösta uppå honom, och alla fromma hjertan skola deraf berömma sig.
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!

< Psaltaren 64 >