< Psaltaren 59 >
1 Ett gyldene klenodium Davids, till att föresjunga, att han icke borto blef, då Saul sände bort, och lät bevara hans hus, på det att han måtte dräpa honom. Fräls mig, min Gud, ifrå mina fiendar, och beskydda mig för dem som sig emot mig sätta.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Fräls mig ifrå de ogerningsmän, och hjelp mig ifrå de blodgiriga.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Ty si, Herre, de vakta efter mina själ; de starke församla sig emot mig, utan min skuld och missgerning.
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 De löpa, utan min skuld, och bereda sig. Vaka upp, och möt mig, och se dertill.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Du, Herre Gud Zebaoth, Israels Gud, vaka upp, och hemsök alla Hedningar. Var ingom nådelig af dem, som sådane förstockade ogerningsmän äro. (Sela)
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Om aftonen låt dem ock tjuta igen, såsom hundar, och löpa omkring i stadenom.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Si, de tala med hvarannan; svärd äro i deras läppar. Ho skulle det höra?
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Men, Herre, du skall le åt dem, och bespotta alla Hedningar.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 För deras magt håller jag mig intill dig; ty Gud är mitt beskärm.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Gud bevisar mig rikeliga sina godhet; Gud låter mig lust se på mina fiendar.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Dräp dem icke, att mitt folk icke förgäter det; men förströ dem med dine magt, Herre, vår sköld, och nedslå dem.
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Deras lära är allsamman synd, och blifva fast i sine högfärd; och predika intet annat än bannor och motsägelse.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 Förgör dem utan alla nåd; förgör dem, så att de intet mer äro, och besinna måga, att Gud är rådandes i Jacob, öfver alla verldena. (Sela)
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 Om aftonen låt dem ock tjuta igen, såsom hundar, och löpa omkring i stadenom.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Låt dem löpa hit och dit efter mat, och tjuta om de icke mätte varda.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Men jag vill sjunga om dina magt, och lofva om morgonen dina godhet; ty du äst mitt beskärm och tillflykt i mine nöd.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Jag vill lofsjunga dig, min tröst; ty du, Gud, äst mitt beskärm, och min gunstige Gud.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.