< Psaltaren 43 >

1 Döm mig, Gud, och uträtta min sak emot det oheliga folk; och fräls mig ifrå de falska och onda menniskor.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Ty du äst, Gud, min starkhet; hvi bortdrifver du mig? Hvi låter du mig gå så sorgse, då min fiende tränger mig?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Sänd ditt ljus och dina sanning, att de leda mig, och föra mig till ditt helga berg, och till dina boning;
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Att jag ingår till Guds altare, till Gud, som min glädje och fröjd är, och tackar dig, Gud, på harpo, min Gud.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Hvad bedröfvar du dig, min själ, och äst så orolig i mig? Hoppas uppå Gud; ty jag skall ännu tacka honom, att han mitt ansigtes hjelp och min Gud är.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psaltaren 43 >