< Psaltaren 31 >

1 En Psalm Davids, till att föresjunga. Herre, uppå dig förtröstar jag, låt mig aldrig på skam komma; fräls mig genom dina rättfärdighet.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Böj din öron till mig, hasteliga hjelp mig; var mig en stark klippa och en borg, att du hjelper mig.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Ty du äst min klippa och min borg; att du dock för ditt Namns skull mig leda och föra ville;
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Att du ville draga mig utu nätet, som de för mig ställt hafva; ty du äst min starkhet.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Uti dina händer befaller jag min anda; du hafver mig förlöst, Herre, du trofaste Gud.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Jag hatar dem som hålla uppå lösaktiga läro; men jag hoppas till Herran.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Jag fröjdar mig, och är glad öfver dina godhet; att du anser mitt elände, och känner mina själ i nödene.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Och du öfvergifver mig icke uti fiendans händer; du sätter mina fötter uppå vidt rum.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Herre, var mig nådelig, ty mig är ångest; mitt ansigte är förfallet för sorgs skull, dertill min själ och min buk.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Ty mitt lefvande är förtärdt vordet af bedröfvelse, och mine år af suckande; min kraft är igenom mina missgerning förfallen, och min ben äro försmäktade.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Det går mig så illa, att jag är en stor försmädelse vorden minom grannom, och en styggelse minom kändom; de som mig se på gatone, de fly för mig.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Jag är förgäten af hjertat, såsom en döder; jag är vorden såsom ett sönderslaget kärile.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Ty månge försmäda mig illa, så att hvar man skyr vid mig; de rådslå med hvarannan om mig, och akta taga mig lifvet bort.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 Men jag, Herre, hoppas uppå dig, och säger: Du äst min Gud.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Min tid står i dina händer; hjelp mig utu mina fiendars hand, och ifrå dem som mig förfölja.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Låt ditt ansigte lysa öfver din tjenare; hjelp mig genom dina godhet.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Herre, låt mig icke till skam varda, ty jag åkallar dig; de ogudaktige varde till skam, och tystade i helvete. (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 Tystne de falske munnar, som tala emot den rättfärdiga hårdeliga, högmodiga och hånliga.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Huru stor är din godhet, den du dem, som dig frukta, bevarat hafver; och bevisar dem, som trösta uppå dig, inför menniskors barn!
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Du förgömmer dem hemliga när dig för hvars mans trug; du förskyler dem i hyddone för de trätosamma tungor.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Lofvad vare Herren, att han mig en underlig godhet bevisat hafver, i enom fastom stad.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Ty jag sade i mine häpenhet: Jag är bortdrifven ifrå dine ögon; likväl hörde du mine böns röst, då jag till dig ropade.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Älsker Herran, alle hans helige. Herren bevarar de trogna, och vedergäller dem rikeliga, som högmod öfva.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Varer tröste och oförfärade, alle I, som Herran förbiden.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Psaltaren 31 >