< Psaltaren 29 >

1 En Psalm Davids. Bärer fram Herranom, I väldige; bärer fram Herranom äro och starkhet.
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Bärer fram Herranom hans Namns äro; tillbedjer Herran i heligo prydning.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 Herrans röst går på vattnen; ärones Gud dundrar; Herren på stor vatten.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 Herrans röst går med magt; Herrans röst går härliga.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 Herrans röst sönderbryter cedrer; Herren sönderbryter cedrer i Libanon;
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 Och låter dem springa såsom en kalf; Libanon och Sirion, såsom en ung enhörning.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 Herrans röst afhugger såsom en eldslåge.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 Herrans röst berörer öknena; Herrans röst berörer öknena Kades.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 Herrans röst berörer hinderna, och blottar skogarna; och i hans tempel skall hvar och en säga honom äro.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Herren sitter till att göra ena flod, och Herren blifver en Konung i evighet.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Herren skall gifva sino folke kraft; Herren skall välsigna sitt folk med frid.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psaltaren 29 >