< Psaltaren 28 >

1 En Psalm Davids. När jag ropar till dig, Herre, min tröst, så tig mig icke; på det, när du tiger, jag icke varder dem lik, som i kulona fara.
Salimo la Davide. Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa; musakhale osamva kwa ine. Pakuti mukapitirira kukhala chete, ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
2 Hör mine böns röst, när jag ropar till dig; när jag upplyfter mina händer till din helga chor.
Imvani kupempha chifundo kwanga pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize, pomwe ndikukweza manja anga kuloza ku malo anu oyeretsetsa.
3 Drag mig icke bort ibland de ogudaktiga, och ibland de ogerningsmän, som vänliga tala med sin nästa, och hafva ondt i hjertat.
Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa, pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa, amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.
4 Gif dem efter sina gerningar, och efter sitt onda väsende; gif dem efter sina händers verk; betala dem det de förtjent hafva.
Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo ndi ntchito zawo zoyipa; abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.
5 Ty de vilja icke akta uppå Herrans gerningar, eller uppå hans händers verk; derföre skall han nederslå, och icke uppbygga dem.
Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova, ndi zimene manja ake anazichita, Iye adzawakhadzula ndipo sadzawathandizanso.
6 Lofvad vare Herran; ty han hafver hört mine böns röst.
Matamando apite kwa Yehova, popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.
7 Herren är min starkhet, och min sköld; uppå honom hoppades mitt hjerta, och mig är hulpet; och mitt hjerta är gladt, och jag vill tacka honom med mine viso.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa; mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa. Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.
8 Herren är deras starkhet; han är den starke, som sin smorda hjelper.
Yehova ndi mphamvu ya anthu ake, linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.
9 Hjelp ditt folk, och välsigna ditt arf, och föd dem, och upphöj dem till evig tid.
Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu; mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

< Psaltaren 28 >