< Psaltaren 27 >

1 En Psalm Davids. Herren är mitt ljus och min helsa; för hvem skall jag frukta mig? Herren är mins lifs kraft; för hvem skulle jag grufva mig?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Derföre, om de onde mine motståndare och fiender till mig vilja, till att fräta mitt kött, måste de stöta sig och falla.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Om än en här lade sig emot mig, så fruktade sig ändå mitt hjerta intet; om en strid hofve sig upp emot mig, så förlåter jag mig uppå honom.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 Ett beder jag af Herranom, det hade jag gerna; att jag i Herrans hus blifva må i alla mina lifsdagar, till att skåda den sköna Herrans Gudstjenst, och besöka hans tempel.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Ty han öfvertäcker mig i sine hyddo i ondom tid; han förgömmer mig hemliga i sitt tjäll, och upphöjer mig på ene klippo;
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 Och skall nu upphöja mitt hufvud öfver mina fiendar, som omkring mig äro; så vill jag i hans hyddo lof offra; jag vill sjunga och lofsäga Herranom.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Herre, hör mina röst, när jag ropar; var mig nådelig, och hör mig.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 Mitt hjerta håller dig ditt ord före: I skolen söka mitt ansigte; derföre söker jag ock, Herre, ditt ansigte.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Fördölj icke ditt ansigte för mig, och bortdrif icke din tjenare i vredene; ty du äst min hjelp; öfvergif mig icke, och drag icke handena ifrå mig, Gud, min salighet.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Ty min fader och min moder öfvergifva mig; men Herren upptager mig.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Herre, visa mig din väg, och led mig på den rätta stigen, för mina fiendars skull.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Gif mig icke uti mina fiendars vilja; ty falsk vittne stå emot mig, och göra mig orätt skamlöst.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Men jag tror dock, att jag se skall Herrans goda, uti de lefvandes lande.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Förbida Herran; var tröst och oförfärad, och förbida Herran.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.

< Psaltaren 27 >