< Psaltaren 17 >
1 En bön Davids. Herre, hör rätthetena; gif akt uppå mitt rop, förnim mina bön, den icke utaf en falsk mun går.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Tala du i mine sak, och se du uppå hvad rätt är.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Du pröfvar mitt hjerta, och besöker det om nattena, och ransakar mig, och finner intet; jag hafver satt mig före, att min mun icke öfverträda skall.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Jag förvarar mig i dina läppars orde, för menniskors gerningar, på mördarens väg.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Behåll min gång på dinom stigom, att min steg icke slinta.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Jag ropar till dig, att du Gud ville höra, mig; böj din öron till mig, hör mitt tal.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Bevisa, dina underliga godhet, du, deras Frälsare, som trösta uppå dig, emot dem som sig emot dina högra hand sätta.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Bevara mig såsom en ögnasten; beskärma mig under dina vingars skugga;
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 För de ogudaktiga, som mig förhärja; för mina ovänner, som efter mina själ stå allt omkring.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Deras fete hålla tillsamman; de tala med sin mun stor ord.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Hvar vi gå, så äro de kringom oss; sina ögon ställa de derefter, att de måga slå oss till jordena;
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Såsom ett lejon, som rof begärar; såsom ett ungt lejon, som i kulone sitter.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Herre, statt upp, öfverfall honom, och nederslå honom; undsätt mina själ ifrå de ogudaktiga, med ditt svärd;
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 Ifrå dine hands menniskom, Herre, ifrå denne verldenes menniskom, hvilka sin del hafva medan de lefva; dem du buken fyller med dina håfvor; de der barn nog hafva, och låta sina återlefvor sinom barnom.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Men jag vill skåda ditt ansigte i rättfärdighet; jag vill mätt varda, när jag uppvakar efter ditt beläte.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.