< Psaltaren 144 >
1 En Psalm Davids. Lofvad vare Herren, min tröst, den mina händer lärer strida, och mina finger örliga;
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
2 Min barmhertighet och min borg, mitt beskärm och min hjelpare, min sköld, på den jag tröster; den mitt folk under mig tvingar;
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
3 Herre, hvad är menniskan, att du så låter dig vårda om henne; och menniskones son, att du så aktar uppå honom?
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
4 Är dock menniskan lika som intet. Hennes tid går bort såsom en skugge.
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
5 Herre, böj din himmel, och stig härned; tag uppå bergen, att de ryka.
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
6 Låt ljunga, och förströ dem; skjut dina skott, och förskräck dem.
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
7 Sänd dina hand af höjdene, och förlossa mig, och fräls mig ifrå stor vatten, ifrå de främmande barnas händer;
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
8 Hvilkas lära är onyttig, och deras gerningar falska.
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
9 Gud, jag vill sjunga dig en ny viso; jag vill spela dig på psaltare af tio stränger;
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 Du, som gifver Konungomen seger, och förlöser din tjenare David ifrå dens ondas mordsvärd.
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
11 Förlös mig ock, och hjelp mig ifrå de främmande barnas hand; hvilkas lära är onyttig, och deras gerningar falska;
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
12 Att våre söner måga uppväxa i deras ungdom, såsom plantor; och våra döttrar, såsom beprydde svalar, såsom palats;
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 Och våra visthus fulle vara, de der spisning utgifva kunna, den ena efter den andra; att våra får måga bära tusend och hundrade tusend, i våra afvelsgårdar;
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
14 Att våre oxar måga mycket arbete göra; att ingen skade, ingen olycka eller klagan på våra gator är.
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
15 Saligt är det folk, hvilko alltså går; men saligt är det folk, hvilkets Gud Herren är.
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.