< Psaltaren 137 >

1 Vid de älfver i Babel såte vi och grete, då vi på Zion tänkte.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Våra harpor hängde vi på pilträ, som der äro.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Ty der bådo de oss sjunga, som oss fångna höllo, och i vår gråt glade vara: Sjunger oss ena af Zions Visor.
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Huru skulle vi sjunga Herrans viso i främmande land?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Om jag förgäter dig, Jerusalem, så varde min högra hand förgäten.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Min tunga låde vid min gom, om jag icke tänker uppå dig; om jag icke låter Jerusalem min högsta glädje vara.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Herre, mins uppå Edoms barn, på Jerusalems dag; de der säga: Slår ned, slår ned i grund.
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Du förstörda dotter Babel, säll är den dig vedergäller, såsom du oss gjort hafver.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Säll är den, som dina unga barn tager, och slår dem emot stenen.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psaltaren 137 >