< Psaltaren 135 >

1 Halleluja. Lofver Herrans Namn; lofver, I Herrans tjenare;
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 I som stån i Herrans hus, uti vår Guds gårdar.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Lofver Herran, ty Herren är god; lofsjunger hans Namn, ty det är ljufligit.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Ty Herren hafver utvalt sig Jacob; Israel till sin egendom.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Ty jag vet, att Herren är stor; och vår Herre för alla gudar.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Allt det Herren vill, det gör han, i himmelen, på jordene, i hafvet, och i all djup;
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Den der låter skyarna uppgå af jordenes ända; den der ljungelden gör, samt med regnet; den der vädret utu hemlig rum komma låter;
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Den der förstfödingen slog uti Egypten, både af menniskor och af boskap;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Och lät sina tecken och under komma öfver dig, Egypti land, öfver Pharao och alla hans tjenare;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Den mång folk slog, och drap mägtiga Konungar:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon, de Amoreers Konung, och Og, Konungen i Basan, och all Konungarike i Canaan;
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Och gaf deras land till arfs, till arfs sino folke Israel.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Herre, ditt Namn varar i evighet; din åminnelse, Herre, varar förutan ända.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Ty Herren skall döma sitt folk, och vara sina tjenare nådelig.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 De Hedningars gudar äro silfver och guld, med menniskors händer gjorde.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 De hafva mun, och tala intet; de hafva ögon, och se intet.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 De hafva öron, och höra intet, och ingen ande är i deras mun.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 De som sådana göra, äro lika så; alle de som hoppas på dem.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Israels hus lofve Herran; lofver Herran, I af Aarons hus.
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 I af Levi hus, lofver Herran; I som frukten Herran, lofver Herran.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Lofvad vare Herren af Zion, den i Jerusalem bor. Halleluja.
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psaltaren 135 >