< Psaltaren 119 >

1 Salige äro de som utan vank lefva, de som i Herrans lag vandra.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Salige äro de som hans vittnesbörd hålla; de som af allo hjerta söka honom.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Ty de som på hans vägom vandra, de göra intet ondt.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Du hafver budit, att hålla dina befallningar fliteliga.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 O! att mitt lif hölle dina rätter med fullt allvar.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 När jag skådar uppå all din bud, så kommer jag icke på skam.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Jag tackar dig af rätt hjerta, att du lärer mig dina rättfärdighets rätter.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Dina rätter vill jag hålla; öfvergif mig dock aldrig.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Huru skall en yngling sin väg ostraffeliga gå? När han håller sig efter din ord.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Jag söker dig af allo hjerta; Låt mig icke fela om din bud.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Jag behåller din ord i mitt hjerta, på det jag icke skall synda emot dig.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Lofvad vare du, Herre; lär mig dina rätter.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Jag vill med mina läppar förtälja alla dins muns rätter.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Jag fröjdar mig af dins vittnesbörds väg, såsom af allahanda rikedomar.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Jag talar det du befallt hafver, och ser på dina vägar.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Jag hafver lust till dina rätter, och förgäter icke din ord.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Gör väl med din tjenare, att jag må lefva och hålla din ord.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Öppna mig ögonen, att jag må se under i din lag.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Jag är en gäst på jordene; fördölj icke din bud för mig.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Min själ är all sönderkrossad för trängtans skull, efter dina rätter alltid.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Du näpser de stolta; förbannade äro de som vika ifrå din bud.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Vänd ifrå mig försmädelse och föraktelse; ty jag håller din vittnesbörd.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Sitta ock Förstarna och tala emot mig; men din tjenare talar om dina rätter.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Jag hafver lust till din vittnesbörd; de äro mine rådgifvare.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Min själ ligger i stoft; vederqvick mig efter ditt ord.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Jag förtäljer mina vägar, och du bönhörer mig; lär mig dina rätter.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Undervisa mig dina befallningars väg, så vill jag tala om din under.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Jag grämer mig så att hjertat mig försmäktas; styrk mig efter ditt ord.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Vänd ifrå mig den falska vägen, och unna mig din lag.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Jag hafver utvalt sanningenes väg; dina rätter hafver jag mig föresatt.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Jag håller mig intill din vittnesbörd; Herre, låt mig icke på skam komma.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 När du mitt hjerta tröstar, så löper jag dins buds väg.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Lär mig, Herre, dina rätters väg, att jag må bevara dem intill ändan.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Undervisa mig, att jag må bevara din lag, och hålla dem af allo hjerta.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 För mig in på din buds stig, ty jag hafver der lust till.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Böj mitt hjerta till din vittnesbörd, och icke till girighet.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Vänd bort min ögon, att de icke se efter onyttig läro; utan vederqvick mig på dinom väg.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Låt din tjenare hålla din bud stadeliga för din ord, att jag må frukta dig.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Vänd ifrå mig den försmädelse, som jag fruktar; ty dine rätter äro lustige.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Si, jag begärar dina befallningar; vederqvick mig med dine rättfärdighet.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Herre, låt mig vederfaras dina nåd; dina hjelp efter ditt ord;
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Att jag mina lastare svara må; ty jag förlåter mig uppå ditt ord.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Och tag ju icke ifrå minom mun sanningenes ord; ty jag hoppas uppå dina rätter.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Jag vill hålla din lag allstädes, alltid och evinnerliga.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Och jag vandrar i glädje; ty jag söker dina befallningar.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Jag talar om din vittnesbörd inför Konungar, och blyges intet;
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Och hafver lust till din bud, och de äro mig käre;
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Och lyfter mina händer upp till din bud, de mig kär äro; och talar om dina rätter.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Tänk dinom tjenare uppå ditt ord, på hvilket du låter mig hoppas.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Det är min tröst i mitt elände; ty ditt ord vederqvicker mig.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 De stolte hafva deras gabberi af mig; likväl viker jag icke ifrå din lag.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Herre, när jag tänker, huru du af verldenes begynnelse dömt hafver, så varder jag tröstad.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Jag brinner innan, för de ogudaktiges skull, som din lag öfvergifva.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Dine rätter äro min visa i mino huse.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Herre, jag tänker om nattena på ditt Namn, och håller din lag.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Det är min skatt, att jag dina befallningar håller.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Jag hafver sagt, Herre: Det skall mitt arf vara, att jag dina vägar håller.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Jag beder inför ditt ansigte af allo hjerta; var mig nådelig efter ditt ord.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Jag betraktar mina vägar, och vänder mina fötter till din vittnesbörd.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Jag skyndar mig, och dröjer intet, till att hålla din bud.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 De ogudaktigas rote beröfvar mig; men jag förgäter intet din lag.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Om midnatt står jag upp, till att tacka dig för dina rättfärdighets rätter.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Jag håller mig till alla dem som frukta dig, och dina befallningar hålla.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Herre, jorden är full af dine godhet; lär mig dina rätter.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Du gör dinom tjenare godt, Herre, efter ditt ord.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Lär mig goda seder och förståndighet; ty jag tror dinom budom.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Förr än jag späkt vardt, for jag vill; men nu håller jag ditt ord.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Du äst mild och god; lär mig dina rätter.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 De stolte dikta lögn öfver mig; men jag håller dina befallningar af allt hjerta.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Deras hjerta är fett vordet, såsom flott; men jag hafver lust till din lag.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Det är mig ljuft att du hafver späkt mig, att jag må lära dina rätter.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Dins muns lag är mig täckare, än mång tusend stycke guld och silfver.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Din hand hafver gjort och beredt mig; undervisa mig, att jag må lära din bud.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 De som dig frukta, de se mig, och glädja sig; ty jag hoppas uppå din ord.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Herre, jag vet att dina domar äro rätte, och du hafver troliga späkt mig.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Din nåd vare min tröst, såsom du dinom tjenare lofvat hafver.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Låt mig vederfaras dina barmhertighet, att jag må lefva; ty jag hafver lust till din lag.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Ack! att de stolte måtte komma på skam, som mig med lögn nedertrycka; men jag talar om dina befallningar.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Ack! att de måtte hålla sig till mig, som dig frukta, och känna din vittnesbörd.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Mitt hjerta blifve rättsinnigt i dinom rättom, att jag icke på skam kommer.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Min själ trängtar efter dina salighet; jag hoppas uppå ditt ord.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Min ögon trängta efter ditt ord, och säga: När vill du trösta mig?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Ty jag är såsom en lägel i rök; dina rätter förgäter jag icke.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Huru länge skall din tjenare bida? När vill du dom hålla öfver mina förföljare?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 De stolte grafva mig gropar, hvilka intet äro efter din lag.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Dine bud äro alltsamman sanning; de förfölja mig med lögn, hjelp mig.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 De hade fulltnär förgjort mig på jordene; men jag öfvergifver icke dina befallningar.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Vederqvick mig genom dina nåd, att jag må hålla dins muns vittnesbörd.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Herre, ditt ord blifver evinnerliga, så vidt som himmelen är.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Din sanning varar i evighet; du hafver tillredt jordena, och hon blifver ståndandes.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Det blifver dagliga efter ditt ord; ty all ting måste tjena dig.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Om din lag icke hade min tröst varit, så vore jag förgången i mitt elände.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Jag vill aldrig förgäta dina befallningar; ty du vederqvicker mig med dem.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Jag är din, hjelp mig; ty jag söker dina befallningar.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 De ogudaktige vakta uppå mig, att de måga förgöra mig; men jag aktar uppå din vittnesbörd,
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Jag hafver på all ting en ända sett; men ditt bud är varaktigt.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Huru hafver jag din lag så kär; dageliga talar jag derom.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Du gör mig med ditt bud visare, än mina fiender äro; ty det är evinnerliga min skatt.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Jag är lärdare, än alle mine lärare; ty din vittnesbörd äro mitt tal.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Jag är förståndigare, än de gamle; ty jag håller dina befallningar.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Jag förtager minom fotom alla onda vägar, att jag må hålla din ord.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Jag viker icke ifrå dina rätter; ty du lärer mig.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Din ord äro minom mun sötare än hannog.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Ditt ord gör mig förståndigan; derföre hatar jag alla falska vägar.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Ditt ord är mina fötters lykta, och ett ljus på minom vägom.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Jag svär, och vill hållat, att jag dina rättfärdighets rätter hålla vill.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Jag är svårliga plågad; Herre, vederqvick mig efter ditt ord.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Låt dig behaga, Herre, mins muns välviljoga offer, och lär mig dina rätter.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Jag bär mina själ i mina händer alltid, och jag förgäter icke din lag.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 De ogudaktige sätta mig snaror; men jag far icke vill ifrå dina befallningar.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Din vittnesbörd äro mitt eviga arf; ty de äro mins hjertas fröjd.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Jag böjer mitt hjerta till att göra efter dina rätter alltid och evinnerliga.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Jag hatar de ostadiga andar, och älskar din lag.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Du äst mitt beskärm och sköld; jag hoppas uppå ditt ord.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Viker ifrå mig, I onde; jag vill hålla min Guds bud.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Uppehåll mig igenom ditt ord, att jag må lefva; och låt mig icke på skam komma med mitt hopp.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Stärk mig, att jag må blifva salig; så vill jag alltid lust hafva till dina rätter.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Du förtrampar alla dem som villa gå om dina rätter; ty deras bedrägeri är alltsammans lögn.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Du bortkastar alla ogudaktiga på jordene som slagg; derföre älskar jag din vittnesbörd.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Jag fruktar mig för dig, så att mitt kött skälfver; och förskräcker mig for dina rätter.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Jag aktar uppå rätt och rättfärdighet; öfvergif mig icke dem som mig öfvervåld göra vilja.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Beskärma du din tjenare, och tröst honom, att de stolte icke göra mig öfvervåld.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Mina ögon trängta efter dina salighet, och efter dine rättfärdighets ord.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Handla med dinom tjenare efter dina nåd; och lär mig dina rätter.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Jag är din tjenare; undervisa mig, att jag må känna din vittnesbörd.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Det är tid, att Herren gör der något till; de hafva omintetgjort din lag.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Derföre älskar jag din bud, öfver guld och öfver fint guld.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Derföre håller jag rätt fram i alla dina befallningar; jag hatar allan falskan väg.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Underliga äro din vittnesbörd, derföre håller dem min själ.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 När ditt ord uppenbaradt varder, så fröjdar det, och gör de enfaldiga visa.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Jag öppnar min mun, och begärar din bud; ty mig längtar efter dem.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Vänd dig till mig, och var mig nådelig, såsom du plägar göra dem som ditt Namn älska.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Låt min gång viss vara i dino orde, och låt ingen orätt öfver mig råda.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Förlös mig ifrå menniskors orätt; så vill jag hålla dina befallningar.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Låt ditt ansigte lysa öfver din tjenare, och lär mig dina rätter.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Mine ögon flyta med vatten, att man icke håller din lag.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Herre, du äst rättfärdig, och rätt är ditt ord.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Du hafver dina rättfärdighets vittnesbörd, och sanningena hårdeliga budit.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Jag hafver när harmats till döds, att mine ovänner hafva din ord förgätit.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Ditt ord är väl bepröfvadt, och din tjenare hafver det kärt.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Jag är ringa och föraktad; men jag förgäter icke dina befallningar.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Din rättfärdighet är en evig rättfärdighet, och din lag är sanning.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Ångest och nöd hafva drabbat uppå mig; men jag hafver lust till din bud.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Dins vittnesbörds rättfärdighet är evig; undervisa mig, så lefver jag.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Jag ropar af allo hjerta, bönhör mig, Herre, att jag må hålla dina rätter.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Jag ropar till dig, hjelp mig, att jag må hålla din vittnesbörd.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Jag kommer bittida, och ropar; uppå ditt ord hoppas jag.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Jag vakar bittida upp, att jag må handla om din ord.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Hör mina röst efter dina nåde: Herre, vederqvick mig efter dina rätter.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Mine arge förföljare vilja till mig, och äro långt ifrå din lag.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Herre, du äst hardt när, och din bud äro alltsamman sanning.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Men jag vet det långt tillförene, att du din vittnesbörd evinnerliga grundat hafver.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Se uppå mitt elände, och fräls mig; hjelp mig ut; förty jag förgäter icke din lag.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Uträtta min sak, och förlossa mig; vederqvick mig igenom ditt ord.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Saligheten är långt ifrå de ogudaktiga; ty de akta intet dina rätter.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Herre, din barmhertighet är stor; vederqvick mig efter dina rätter.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Mine förföljare och ovänner äro månge; men jag viker icke ifrå din vittnesbörd.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Jag ser de föraktare, och det gör mig ondt, att de icke hålla din ord.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Si, jag älskar dina befallningar; Herre, vederqvick mig efter din nåd.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Ditt ord hafver af begynnelsen varit sanning; alle dine rättfärdighets rätter vara evinnerliga.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Förstarna förfölja mig utan sak, och mitt hjerta fruktar sig för din ord.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Jag gläder mig öfver din ord, såsom en den stort byte får.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Lögnene är jag hätsk, och stygges dervid, men din lag hafver jag kär.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Jag lofvar dig sju resor om dagen, för dine rättfärdighets rätters skull.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Stor frid hafva de som din lag älska, och de skola icke stappla.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Herre, jag väntar efter din salighet, och gör efter din bud.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Min själ håller din vittnesbörd, och hafver dem mycket kär.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Jag håller dina befallningar, och dina vittnesbörder; ty alle mine vägar äro för dig.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Herre, låt min klagan för dig komma; undervisa mig efter ditt ord.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Låt mina bön komma för dig; fräls mig efter ditt ord.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Mine läppar skola lofva, när du lärer mig dina rätter.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Min tunga skall tala om ditt ord; ty all din bud äro rätt.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Låt dina hand vara mig biståndiga; ty jag hafver utkorat dina befallningar.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Herre, jag längtar efter din salighet, och hafver lust till din lag.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Låt mina själ lefva, att hon må lofva dig, och dine rätter hjelpa mig.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Jag är såsom ett villfarande och borttappadt får; sök din tjenare, ty jag förgäter icke din bud.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psaltaren 119 >