< Psaltaren 114 >

1 Då Israel ut ur Egypten drog, Jacobs hus ifrå främmande folk.
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Då vardt Juda hans helgedom, Israel hans välde.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Hafvet såg det, och flydde; Jordanen vände tillbaka.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Bergen sprungo såsom lamb; högarna såsom ung får.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Hvad var dig, du haf, att du flydde; och du Jordan, att du tillbakavände?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 I berg, att I sprungen såsom lamb; I högar, såsom ung får?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 För Herranom bäfvade jorden, för Jacobs Gud;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Den bergsklipporna förvandlar uti vattusjöar, och stenen i vattukällor.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psaltaren 114 >