< Psaltaren 104 >

1 Lofva Herran, min själ; Herre, min Gud, du äst ganska härlig, du äst dägelig och allstinges väl beprydd.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Ljus är din klädnad, som du uppå hafver; du utsträcker himmelen såsom ett tapet.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 Du hvälfver honom ofvan med vatten; du far i skyn såsom i en vagn, och går på vädrens vingar;
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Du, som gör dina Änglar till väder, och dina tjenare till eldslåga;
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Du, som grundar jordena på hennes botten, så att hon blifver i evig tid.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Med djupet betäcker du henne, såsom med ett kläde, och vatten stå öfver bergen.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Men för ditt näpsande fly de; för ditt dundrande fara de bort.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Bergen resa högt upp, och dalarna sätta sig ned i det rum, som du dem skickat hafver.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Du hafver satt ett mål, der komma de intet öfver; och måga icke åter betäcka jordena.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Du låter källor uppbrista i dalomen, så att vatten emellan bergen flyta;
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Att all djur på markene måga dricka, och vildåsnarna sin törst släcka.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 När dem sitta himmelens foglar, och sjunga på qvistarna.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Du fuktar bergen ofvanefter; du gör landet fullt med frukt, den du förskaffar.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Du låter gräs växa för boskapen, och säd menniskomen till nytto; att du skall låta komma bröd utaf jordene;
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 Och att vin skall fröjda menniskones hjerta, och hennes ansigte dägeligit varda af oljo, och bröd styrka menniskones hjerta;
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 Att Herrans trä skola full med must stå; de cedreträ på Libanon, som han planterat hafver.
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 Der hafva foglarna sitt näste, och hägrar bo uppe i furoträn.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 De höga berg äro de stengetters tillflykt, och stenklyfterna de kunilers.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Du gör månan, till att derefter skifta året; solen vet sin nedergång.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Du gör mörker, att natt varder; då draga sig all vilddjur ut;
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 De unga lejon, som ryta efter rof, och sin mat söka af Gudi;
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Men när solen uppgår, draga de bort, och lägga sig uti sina kulor.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Så går då menniskan ut till sitt arbete, och till sitt åkerverk intill aftonen.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Herre, huru äro din verk så stor och mång! Du hafver visliga skickat dem all, och jorden är full af dina ägodelar.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Hafvet, det så stort och vidt är, der kräla uti, utan tal, både stor och liten djur.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 Der gå skepp; der äro hvalfiskar, som du gjort hafver, att de deruti leka skola.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Allt vänter efter dig, att du skall gifva dem mat i sin tid.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Då du gifver dem, så samla de; när du upplåter dina hand, så varda de med god ting mättade.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Om du fördöljer ditt ansigte, så varda de förskräckte; du tager deras anda bort, så förgås de, och varda åter till stoft igen.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Du låter ut din anda, så varda de skapade, och du förnyar jordenes ansigte.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Herrans ära är evig; Herren hafver behag till sin verk.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 Han ser uppå jordena, så bäfvar hon; han kommer vid bergen, så ryka de.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Jag vill sjunga Herranom i mina lifsdagar, och lofva min Gud, så länge jag är till.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Mitt tal behage honom väl; jag gläder mig af Herranom.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Syndarena hafve en ända på jordene, och de ogudaktige vare icke mer till; lofva, min själ, Herran. Halleluja.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psaltaren 104 >