< Ordspråksboken 29 >
1 Hvilken som emot straff genstörtig är, han skall med hast förderfvad varda, utan all hjelp.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 När de rättfärdige månge äro, så glädes folket; men när den ogudaktige regerar, så suckar folket.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Den som vishet älskar, han gläder sin fader; men den som skökor uppehåller, han mister sina ägodelar.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 En Konung upprätter landet genom rätt; men en girig förderfvar det.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Den som smekrar med sin nästa, han utbreder ett nät för hans fötter.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 När en ond syndar, besnärjer han sig sjelf; men en rättfärdig fröjdar sig, och hafver glädje.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Den rättfärdige känner den fattigas sak; den ogudaktige aktar ingen förnuft.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 De bespottare föra en stad i olycko; men de vise stilla vrede.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 När en vis med en dåra till handel kommer, han vare vred eller glad, så hafver han dock ingen ro.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 De blodgirige hata den fromma; men de rättfärdige vårda sig om hans själ.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 En dåre gjuter sin anda allan ut; men en vis man håller tillbaka.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 En herre, som till lögn lust hafver, hans tjenare äro alle ogudaktige.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Fattige och ockrare bo ibland hvarannan; begges deras ögon upplyser Herren.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 En Konung, som de fattiga troliga dömer, hans säte blifver evigliga beståndandes.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Ris och straff gifver vishet; men ett barn, som hafver sjelfsvåld, skämmer sina moder.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Der månge ogudaktige äro, der äro många synder; men de rättfärdige skola se deras fall.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Tukta din son, så skall han vederqvicka dig, och göra dine själ vällust.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 När Prophetien ute är, så förskingras folket; men väl är honom, som lagen vid magt håller.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 En tjenare låter icke näpsa sig med ordom; förty, om han än förstår det, så tager han sig dock intet deraf.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Ser du en, som snar är till att tala, det är mera hopp uppå en dåra, än uppå honom.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Om en tjenare varder af ungdom kräseliga hållen, så vill han sedan vara en herre.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 En vredsam man kommer träto åstad, och en harmse man gör många synder.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Menniskones högfärd skall omstörta henne; men ära skall upphöja den ödmjuka.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Den som med tjufvar del hafver, hörer bannas; och säger icke till, han hatar sitt lif.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Den som rädes för menniskom, han kommer på fall; men den som sig förlåter uppå Herran, han varder beskyddad.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Månge söka ens Förstas ansigte; men hvars och ens dom kommer af Herranom.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 En orättfärdig man är dem rättfärdigom en styggelse; och den som på en rätt väg är, han är dens ogudaktigas styggelse.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.