< Ordspråksboken 26 >

1 Lika som snö om sommaren, och regn i andene, så höfves icke enom dåra ära.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Lika som en fogel bortfar, och en svala flyger, alltså biter intet en oförtjent banna.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Hästenom en gissel, och åsnanom ett betsel, och dåranom ett ris på ryggen.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Svara icke dåranom efter hans dårskap, att du honom icke lik varder.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Men svara dåranom efter hans dårskap, att han icke skall låta sig tycka, att han är vis.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Den ena sak genom ett galet bådskap beställer, han är såsom en halter på fötterna, och tager skada.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Såsom enom krympling står att dansa, alltså står enom dåra tala om vishet.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Den enom dåra äro tillägger, det är lika som man kastade en ädla sten uppå en stenrösjo.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Ett ordspråk uti ens dåras mun är såsom en törneqvist, den uti ens druckens mans hand stinger.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 En god mästare gör ett ting rätt; men den som en klåpare lejer, honom varder det förderfvadt.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Såsom en hund uppäter sina spyor igen, alltså är en dåre som sin galenskap på nytt bedrifver.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 När du en ser, som sig tycker vis vara, det är mera hopp uppå en dåra, än på honom.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Den late säger: Det är ett ungt lejon på vägenom, och ett lejon på gatone.
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 En later vänder sig i sängene, lika som en dörr på dörrajernen.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Den late gömmer sina hand i barmen, och det varder honom tungt, att han skall bära henne åt munnen.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 En later tycker sig visare vara än sju, som seder lära.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Den som framgår, och blandar sig uti annars kif, han är lika som en, den der drager en hund med öronen.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Lika som en hemliga med skott och pilar skjuter, och dräper;
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 Alltså gör en falsk menniska med sin nästa, och säger sedan: Det var mitt skämt.
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Då intet mer ved är, slocknar elden; och när klaffaren är borta, vänder trätan åter.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Såsom kolen glöd, och veden eld, alltså kommer en trätosam man kif åstad.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Klaffarens ord äro såsom hugg, och de gå igenom hjertat.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 En förgiftig mun, och ondt hjerta, är såsom en lerpotta med silfslagg öfverdragen.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Fienden varder känd vid sitt tal, och när han nalkas, far han med falskhet.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Då han smeker med sitt mjuka tal, tro honom intet; ty sju styggelser äro uti hans hjerta.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Den som hat hemliga håller, till att göra skada, hans ondska skall den meniga man uppenbar varda.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Den ena grop gör, han skall falla deruti; och den en sten välter, uppå honom skall han komma.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 En falsk tunga hatar den henne straffar, och en smeken mun kommer förderf åstad.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Ordspråksboken 26 >