< Ordspråksboken 21 >

1 Konungens hjerta är uti Herrans hand, såsom vattubäcker; och han böjer det hvart han vill.
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Hvar och en tycker sin väg rättan vara; men Herren allena gör hjertan viss.
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Göra väl och rätt är Herranom kärare än offer.
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Högfärdig ögon, och ett stolt sinne, och de ogudaktigas lykta, är synd.
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 En idogs mans anslag draga in ymnoghet; men den som allt för hastig är, han varder fattig.
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Den som en skatt samkar med lögn, honom skall fela; och han skall falla ibland dem som döden söka.
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 De ogudaktigas röfvande skall förskräcka dem; ty de ville icke göra hvad rätt var.
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 Den en främmande väg går, han är vrångvis; men den som går i sine befallning, hans verk är rätt.
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Bättre är bo uti en vrå på taket, än med en trätosam qvinna uti ett stort hus.
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 Dens ogudaktigas själ önskar ondt, och unnar sinom nästa intet godt.
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 När bespottaren straffad varder, varda de fåkunnige vise; och när man underviser en visan, så varder han förnuftig.
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 En rättfärdig håller sig visliga emot dens ogudaktigas hus; men de ogudaktige tänka till att göra skada.
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Den som tillstoppar sin öron för dens fattigas rop, han skall ock ropa, och intet hörd varda.
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 En hemlig gåfva stillar vrede, och en skänk i skötet aldrastörsta ogunst.
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 Det är dem rättfärdiga en glädje, att göra det rätt är; men fruktan blifver dem som illa göra.
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 En menniska, som ifrå klokhetenes väg, hon skall blifva uti de dödas hop.
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 Den som gerna lefver i vällust, han skall blifva fattig; och den der vin och oljo älskar, han varder icke rik.
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 Den ogudaktige måste i dens rättfärdigas stad utgifven varda, och föraktaren för de fromma.
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 Bättre är att bo uti ett öde land, än när en trätosamma och ensinnada qvinno.
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 Uti dens visas hus är en lustig skatt, och olja; men en dåre förtärer det.
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 Den som far efter barmhertighet och godhet, han finner lif, barmhertighet och äro.
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 En vis man vinner de starkas stad, och omstörter hans magt genom hans säkerhet.
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 Den sin mun och tungo bevarar, han bevarar sina själ för ångest.
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 Den som stolt och öfverdådig är, han kallas en lösaktig menniska, den i vredene stolthet bevisar.
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 Den late dör öfver sine önsko; ty hans händer vilja intet göra.
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 Han önskar dagliga; men den rättfärdige gifver, och nekar intet.
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 De ogudaktigas offer är en styggelse; ty det varder i synd offradt.
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 Ett lögnaktigt vittne skall förgås; men den som höra gitter, honom låter man ock tala igen.
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 Den ogudaktige löper igenom med hufvudet; men den der from är, hans väg blifver beståndandes.
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 Ingen vishet, intet förstånd, ingen konst hjelper emot Herran.
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 Hästar varda tillredde till stridsdagen; men segren kommer af Herranom.
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Ordspråksboken 21 >