< Ordspråksboken 19 >

1 En fattig man, den i sine fromhet vandrar, är bättre än en vrång man med sina läppar, den dock en dåre är.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 Der man icke med förnuft handlar, der går det intet väl till; och den som snar är på fötterna, han stöter sig.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 Ens menniskos galenskap förförer hans väg, att hans hjerta emot Herran vredgas.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Gods gör många vänner; men den fattige varder af sinom vännom förlåten.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Ett falskt vittne blifver icke ostraffadt; och den der lögn dristeliga talar, han skall icke undslippa.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Månge vakta uppå Förstans person; och alle äro dens vänner, som skänker gifver.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Den fattiga hata alle hans bröder, ja, ock hans vänner draga sig långt ifrå honom; och den som sig uppå ord förlåter, han får intet.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Den der klok är, han älskar sitt lif; och den förståndige finner godt.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Ett falskt vittne blifver icke ostraffadt; och den der lögn dristeliga talar, han skall förgås.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Dem galna höfves icke väl goda dagar, mycket mindre enom tjenare att råda öfver Förstar.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 Den der tålig är, han är en klok menniska; och det är honom ärligit, att han odygd öfverse kan.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 Konungens ogunst är såsom ens ungs lejons rytande; men hans gunst är såsom dagg på gräs.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 En galen son är sins faders sorg, och en trätosam qvinna ett stadigt drypande.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Hus och ägodelar ärfvas af föräldrom; men en förnuftig hustru kommer af Herranom.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Lathet hafver sömn med sig, och en fåfäng själ skall hunger lida.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 Den som budet bevarar, han bevarar sitt lif; men den sin väg föraktar, han skall dö.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Den som förbarmar sig öfver den fattiga, han lånar Herranom; han skall vedergälla honom godt igen.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Tukta din son, medan något hopp är; men låt icke dina själ dragas till att döda honom;
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Ty stor harm kommer skada åstad; derföre låt honom lös, så kan du mer tukta honom.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Hör råd, och tag vid tuktan, att du sedan må vis varda.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 Mång anslag äro uti ens mans hjerta; men Herrans råd blifver beståndandes.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Menniskona pryder hennes välgerning; och en fattig man är bättre än en ljugare.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 Herrans fruktan fordrar till lifs; och skall mätt varda, att intet ondt skall hemsöka henne.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 Den late gömmer sina hand i barmen, och förer henne icke till munnen igen.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Slår man bespottaren, så blifver den fåkunnige vis; straffar man en förståndigan, så varder han förnuftig.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Den som fadren förlägger, och modrena fördrifver, han är ett skamligit och förbannadt barn.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Låt af, min son, att höra den tuktan, som förer ifrå förnuftig Iäro.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Ett vrångt vittne bespottar domen; och de ogudaktigas mun uppslukar orätthetena.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Bespottarom är straff beredt, och slag på de dårars rygg.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Ordspråksboken 19 >