< 4 Mosebok 36 >
1 Och de öfverste fäderna till Gileads barnas slägte, Machirs sons, hvilken Manasse son var, af Josephs barnas slägte, gingo fram, och talade för Mose, och för Förstarna, öfversta fäderna till Israels barn;
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 Och sade: Käre herre, Herren hafver budit, att man skall utskifta landet Israels barnom till arfvedel genom lott; och du, min herre, hafver budit genom Herran, att man vår broders Zelaphehads arfvedel hans döttrar gifva skall.
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 Om någor af Israels slägte tager dem till hustru, så varder vår faders arfvedel mindre, och så mycket som de hafva, kommer den slägtenes arfvedel till, dit som de komma; och så varder vår arfvedels lott förminskad.
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 När nu Israels barnas klangår kommer, så kommer deras arfvedel till den slägtenes arfvedel, der de äro; så varder vår faders arfvedel förminskad, så mycket som de hafva.
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 Så böd Mose Israels barnom, efter Herrans befallning, och sade: Josephs barnas slägt hafver talat rätt.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 Detta är det som Herren bjuder Zelaphehads döttrar, och säger: Gifte sig hvem de vilja; allenast att de gifta sig in i sina ätt och faders slägte;
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 På det att Israels barnas arfvedel icke skall falla ifrå den ena slägten till den andra; ty hvar och en ibland Israels barn skall hänga intill sitt fädernes slägtes arf.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 Och alla döttrar, som äga arfvedel i Israels barnas slägter, skola gifta sig enom af sins faders slägts ätt; på det hvar och en ibland Israels barn må behålla sins faders arf;
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 Och en arfvedel icke skall falla ifrå den ena slägtene till den andra; utan hvar och en hänge intill sitt arf ibland Israels barnas slägter.
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 Såsom Herren böd Mose, så gjorde Zelaphehads döttrar:
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 Mahela, Thirza, Hogla, Milca och Noa, och gifte sig vid deras faderbroders barn,
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 Af Manasse barnas slägte, Josephs sons; alltså blef deras arfvedel vid ättena och deras faders slägte.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 Desse äro de bud och rätter, som Herren genom Mose böd Israels barnom, på de Moabiters mark, vid Jordan, in mot Jericho.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.