< 4 Mosebok 32 >

1 Rubens barn och Gads barn hade ganska mycken boskap; och de sågo det landet Jaeser och Gilead, att det var beqvämt rum till att föda boskap.
Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
2 Så kommo de, och talade till Mose, och till Presten Eleazar, och till Förstarna i menighetene:
Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
3 Det landet Ataroth, Dibon, Jaeser, Nimra, Hesbon, Eleale, Sebam, Nebo och Beon,
“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
4 Som Herren slagit hade för Israels menighet, är beqvämt till boskap, och vi dine tjenare hafve boskap;
dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
5 Och sade ytterligare: Hafve vi funnit nåde för dig, så gif dinom tjenarom detta landet till eget; och så fare vi intet öfver Jordanen.
Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
6 Mose sade till dem: Skulle edra bröder draga i strid, och I skullen blifva här?
Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
7 Hvi omvänden I Israels barnas hjerta, att de icke skola draga utöfver, uti det land, som Herren dem gifva skall?
Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
8 Alltså gjorde ock edra fäder, då jag sände dem ifrå KadesBarnea, till att skåda landet;
Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
9 Och då de voro komne ditupp, allt intill den bäcken Escol, och sågo landet, omvände de Israels barnas hjerta, så att de icke ville in uti landet, som Herren dem gifva ville.
Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
10 Och Herrans vrede förgrymmade sig på den tiden, och han svor, och sade:
Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
11 Detta folket, som utur Egypten draget är, ifrå tjugu år och deröfver, skola ju icke se det landet, som jag Abraham, Isaac och Jacob svorit hafver; derföre, att de mig icke troliga efterföljt hafva;
‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
12 Undantagnom Caleb, Jephunne son, den Kenisiten, och Josua, Nuns son; ty de hafva Herranom troliga efterföljt.
Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
13 Så förgrymmade sig Herrans vrede öfver Israel, och lät fara dem hit och dit i öknene i fyratio år, intilldess en ände vardt på allt det slägtet, som syndat hade emot Herran.
Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 Och si, I ären inträdde uti edra fäders stad, att syndarena skola vara desto flere, och att I också Herrans vrede och grymhet ännu föröka skullen emot Israel.
“Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
15 Förty om I vänden eder ifrå honom, så varder han ock ännu länger låtandes eder blifva i öknene, och så förderfven I allt detta folket.
Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 Då gingo de fram, och sade: Vi vilje allenast bygga här fägårdar för vår boskap, och städer för vår barn;
Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
17 Men vi vilje väpna oss, och gå framför Israels barn, intilldess vi före dem till deras rum; vår barn skola blifva uti de fasta städer för landsens inbyggares skull.
Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
18 Vi vilje icke vända hemåt, intilldess Israels barn intaga hvar sitt arf;
Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
19 Ty vi vilje intet ärfva med dem på hinsidan Jordan; utan vårt arfvegods må vara på denna sidone Jordan österut.
Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 Mose sade till dem: När I det göra viljen, att I rusten eder till strid för Herranom;
Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
21 Så drager öfver Jordan för Herranom, hvilken som helst ibland eder väpnader är, tilldess I utdrifven hans fiendar ifrå hans ansigte;
ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
22 Och landet blifver undergifvet för Herranom; sedan skolen I vända om, och oskyldige vara för Herranom, och för Israel; och skolen så hafva detta landet till eget för Herranom.
dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 Men om I det icke göra viljen, si, så varden I syndande emot Herran, och varden edra synder förnimmande, då de begripa eder.
“Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
24 Så bygger nu städer för edor barn, och fägårdar för edor boskap; och görer som I sagt hafven.
Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 Gads barn och Rubens barn sade till Mose: Dine tjenare skola göra såsom min herre budit hafver.
Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
26 Vår barn, hustrur, håfvor, och all vår boskap skola blifva uti Gileads städer.
Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
27 Men vi dine tjenare vilje alle väpnade draga i stridena för Herranom, såsom min herre sagt hafver.
koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 Då böd Mose för deras skull Prestenom Eleazar, och Josua, Nuns son, och de öfversta fäderna i Israels barnas slägter;
Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
29 Och sade till dem: Om Gads barn och Rubens barn draga öfver Jordan med eder, alle väpnade till strid för Herranom, och landet blifver eder allt undergifvet; så gifver dem det landet Gilead till eget;
Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
30 Men draga de icke med eder väpnade, så skola de ärfva med eder i Canaans lande.
Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 Gads barn och Rubens barn svarade, och sade: Såsom Herren talat hafver till dina tjenare, så vilje vi göra.
Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
32 Vi vilje draga väpnade för Herranom in uti Canaans land, och besitta vårt arfvegods på desso sidone Jordan.
Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 Så gaf Mose Gads barnom, och Rubens barnom, och den halfva slägtene Manasse, Josephs sons, Sihons rike, de Amoreers Konungs, och Ogs rike, Konungens i Basan, landet och städerna i alla gränsor, deromkring.
Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 Då byggde Gads barn Dibon, Ataroth, Aroer,
Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
35 Atroth, Sophan, Jaeser, Jogbeha,
Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
36 Bethnimra och Betharan, bevarada städer och fägårdar.
Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
37 Rubens barn byggde Hesbon, Eleale, Kiriathaim,
Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
38 Nebo, BaalMeon; och förvände namnen; och Sibma; och gåfvo de städer namn, som de byggde.
Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 Och Machirs barn, Manasse sons, drogo till Gilead, och vunno den, och fördrefvo de Amoreer, som derinne voro.
Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
40 Då gaf Mose Machir, Manasse sone, Gilead; och han bodde deruti.
Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
41 Men Jair, Manasse son, drog bort, och vann deras byar, och kallade dem HavothJair.
Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
42 Nobah drog åstad, och vann Kenath med dess döttrar, och kallade dem Nobah efter sitt namn.
Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.

< 4 Mosebok 32 >