< 4 Mosebok 31 >
1 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Hämna Israels barn öfver de Midianiter, att du sedan församkar dig till ditt folk.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 Så talade Mose med folket, och sade: Väpner män af eder till härs emot de Midianiter, att de hämnas Herran öfver de Midianiter;
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Utu hvart slägte ett tusend, så att I skicken i hären af alla Israels slägter.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 Och de togo af Israels tusender, ju tusende af hvart slägtet, tolftusende väpnade till härs.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 Och Mose skickade dem med Pinehas, Prestens Eleazars son, i här, och de helga tygen, och de klangtrummeter i hans hand.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 Och de förde hären emot de Midianiter, såsom Herren hade budit Mose; och slogo ihjäl allt det som mankön var.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 Dertill slogo de de Midianiters Konungar, med deras slagna, nämliga Evi, Rekem, Zur, Hur och Reba, de fem Midianiters Konungar; Bileam, Beors son, slogo de ock med svärd.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 Och Israels barn togo till fångar de Midianiters qvinnor med deras barn; all deras boskap, alla deras håfvor, och allt deras gods skinnade de;
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 Och uppbrände med eld alla deras städer, deras boningar och alla borger;
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Och togo allt rof, och allt det till tagandes var, både menniskor och boskap;
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 Och hade det till Mose, och till Presten Eleazar, och till menighetena af Israels barn, nämliga de fångar och den tagna boskapen, och det skinnade godset, uti lägret på de Moabiters mark, som ligger vid Jordan emot Jericho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Och Mose och Eleazar Presten, och alle Förstarna för menighetene, gingo emot dem ut för lägret.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Och Mose vardt vred på härens höfvitsmän, som höfvitsmän voro öfver tusende, och öfver hundrade, och kommo utu hären och stridene;
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Och sade till dem: Hafven I låtit alla qvinnor lefva?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Si, hafva icke de förvändt Israels barn, genom Bileams råd, till att synda emot Herran på Peor; och en plåga öfvergick Herrans menighet?
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Så slår nu ihjäl allt det som mankön är ibland barnen, och alla de qvinnor, som man känt och när legat hafva.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 Men all pigobarn, som icke ännu man känt, eller när legat hafva, dem låter för eder lefva.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 Och ligger utanför lägret i sju dagar, alle som någon slagit, eller den slagen var vederkommit hafven, på det I skolen rena eder på tredje och sjunde dagen; samt med dem som I till fångar gripit hafven.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Och all kläder, och all tyg af skinn, och allt skinnverk, och all träkäril skolen I skär göra.
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Och Presten Eleazar sade till krigsfolket, som i stridene varit hade: Detta är lagen, som Herren hafver budit Mose:
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Guld, silfver, koppar, jern, tenn och bly;
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 Och allt det som eld lider, skolen I gå låta genom eld, och rena det, att det med stänkevattnena skärt varder; men allt det som icke lider eld, skolen I låta gå genom vatten;
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 Och skolen två eder kläder på sjunde dagen, så varden I rene; sedan skolen I komma i lägret.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Tag summona af fångarnas rof, både af menniskor och af boskap, du och Eleazar Presten, och de öfverste fäderna i menighetene;
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 Och gif dem hälftena, som utgingo i hären, och stridt hafva, och andra hälftena menighetene.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Och du skall häfoffra Herranom af stridsmännernas del, som i hären voro, ju af femhundrade ena själ, både i menniskor, fä, åsnar och får.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 Af deras hälfte skall du taga det, och få det Prestenom Eleazar, till att häfoffra det Herranom.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 Men af den hälften, som Israels barn tillkommer, skall du ju af femtio taga ett stycke, både af menniskor, fä, åsnar och får, och af allom fänad, och skall gifva det Leviterna, som taga vara på Herrans tabernakels vakt.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 Och Mose, och Eleazar Presten, gjorde såsom Herren hade budit Mose.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 Och det öfriga bytet, som krigsfolket röfvat hade, var sexhundradetusend, fem och sjutio tusend får;
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 Tu och sjutio tusend nöt;
Ngʼombe 72,000,
34 Ett och sextio tusend åsnar;
abulu 61,000,
35 Och qvinnfolk, som icke hade känt man eller när legat, tu och tretio tusend själar.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 Och den hälften, som dem tillkom, som i stridene varit hade, var i talet trehundradetusend, sju och tretio tusend, och femhundrade får;
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 Deraf vordo Herranom sexhundrade fem och sjutio får.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 Item sex och tretio tusend nöt; deraf vordo Herranom tu och sjutio.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Item tretiotusend och femhundrade åsnar; deraf vordo Herranom en och sextio.
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Item menniskors själar, sextontusend själar; deraf vordo Herranom två och tretio.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 Och Mose fick det Herrans häfoffret Prestenom Eleazar, såsom Herren honom budit hade.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 Men den andra hälften, som Mose Israels barnom tillbytt hade ifrå krigsmännerna;
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 Nämliga den hälften, som menighetene tillkom, var ock trehundradetusend, sju och tretio tusend, femhundrade får;
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 Sex och tretio tusend nöt;
ngʼombe 36,000,
45 Tretiotusend och femhundrade åsnar;
abulu 30,500,
46 Och sextontusend menniskors själar.
anthu 16,000.
47 Och Mose tog af denna hälftene, som Israels barnas var, ju ett stycke af femtio, både af fänaden och af menniskor, och fick det Leviterna, som togo vara på Herrans tabernakels vakt; såsom Herren hade budit Mose.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Och de som höfvitsmännerna voro öfver de tusend i krigsfolket, nämliga öfver tusend, och öfver hundrade, gingo fram till Mose;
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 Och de sade till honom: Dine tjenare hafva tagit summona af krigsfolket, som under våra händer varit hafva, och der fattas icke en.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Derföre bäre vi Herranom gåfvor, hvad som hvar och en funnit hafver af gyldene tyg, kedjor, armsmide, ringar, örnaringar och spann, att våra själar måga varda försonada för Herranom.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 Och Mose med Prestenom Eleazar tog af dem guldet i allahanda tyg.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 Och allt gulds häfoffer, som de Herranom häfoffrade, var sextontusend, sjuhundrade och femtio siklar, af höfvitsmännerna öfver tusend, och öfver hundrade.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 Förty krigsfolket hade röfvat hvar och en för sig.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 Och Mose med Prestenom Eleazar tog guldet af höfvitsmännerna öfver tusend, och öfver hundrade, och båro det in uti vittnesbördsens tabernakel, Israels barnom till en åminnelse för Herranom.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.