< 4 Mosebok 29 >

1 Och den förste dagen i sjunde månadenom skall ibland eder kallas helig, att I sammankommen; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå; det är eder trummetandes dag.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Och I skolen göra bränneoffer till en söt lukt Herranom, en ungan stut, en vädur, sju årsgamla lamb utan vank.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Dertill deras spisoffer, tre tiungar semlomjöl, blandadt med oljo, till stuten, två tiungar till väduren;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 En tiung på hvart och ett af de sju lamben;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Och en getabock till syndoffer, till att försona eder;
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Förutan månadens bränneoffer, och dess spisoffer, och förutan det dagliga bränneoffret med dess spisoffer, och med deras drickoffer, efter deras sätt, till en söt lukt; det är ett offer Herranom.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Den tionde dagen i denna sjunde månadenom skall ock när eder kallas helig, att I sammankommen; och I skolen späka edra kroppar, och intet arbete deruppå göra;
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Utan offra bränneoffer Herranom till en söt lukt, en ungan stut, en vädur, sju årsgamla lamb utan vank;
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Med deras spisoffer, tre tiungar semlomjöl, blandade med oljo, till stuten, två tiungar till väduren;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Och en tiung på hvart och ett af de sju lamben.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Dertill en getabock till syndoffer, förutan försoningens syndoffer, och det dagliga bränneoffret med sitt spisoffer, och med deras drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Den femtonde dagen i den sjunde månaden skall kallas helig när eder, att I sammankommen; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå, och I skolen hålla Herranom helg i sju dagar;
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Och skolen göra bränneoffer till en söt lukts offer Herranom, tretton unga stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Med deras spisoffer, tre tiungar semlomjöl, blandadt med oljo, till hvar och en af de tretton stutar, två tiungar uppå hvar väduren af de två;
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Och en tiung uppå hvart och ett af de fjorton lamben.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret med sitt spisoffer och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 På den andra dagen, tolf unga stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret med sitt spisoffer, och med deras drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 På tredje dagen, ellofva stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret, med sitt spisoffer och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 På fjerde dagen, tio stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret med sitt spisoffer, och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 På femte dagen, nio stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret, med sitt spisoffer, och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 På sjette dagen, åtta stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret, med sitt spisoffer, och sitt drickoffer.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 På sjunde dagen sju stutar, två vädrar, fjorton årsgamla lamb utan vank;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Med deras spisoffer och drickoffer, till stutarna, till vädrarna, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Dertill en getabock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret, med sitt spisoffer, och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 På den åttonde skall vara församlingenes dag; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Och skolen offra bränneoffer till en söt lukts offer Herranom; en stut, en vädur, sju årsgamla lamb, utan vank;
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Med deras spisoffer och drickoffer, till stuten, till väduren, och till lamben, i deras tal efter sättet.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Dertill en bock till syndoffer, förutan det dagliga bränneoffret, med sitt spisoffer och sitt drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Detta skolen I göra Herranom i edra högtider, undantagno det I lofven och friviljoge gifven till bränneoffer, spisoffer, drickoffer och tackoffer.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Och Mose sade Israels barnom allt det Herren honom budit hade.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< 4 Mosebok 29 >