< 4 Mosebok 21 >

1 Och då den Cananeen, Konungen i Arad, som söderut bor, hörde att Israel inkom genom spejares väg, stridde han emot Israel, och förde några af dem fångna.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
2 Då lofvade Israel Herranom ett löfte, och sade: Om du gifver detta folket under mina hand, så skall jag gifva deras städer tillspillo.
Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
3 Och Herren hörde Israels bön, och gaf dem de Cananeer, och de gjorde dem tillspillo med deras städer; och kallade det rummet Horma.
Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
4 Sedan drogo de ifrå berget Hor, på den vägen åt röda hafvet, att de skulle draga omkring de Edomeers land. Och folket vardt ledse på vägen.
Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
5 Och folket talade emot Gud, och emot Mose: Hvi hafver du fört oss utur Egypten, att vi skulle dö i öknene? Ty här är hvarken bröd eller vatten, och vår själ vämjar öfver denna lösa maten.
ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
6 Då sände Herren ibland folket brännande ormar; de beto folket, så att mycket folk i Israel blef dödt.
Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
7 Så kommo de till Mose, och sade: Vi hafve syndat, att vi emot Herran och emot dig talat hafve; bed Herran, att han tager dessa ormarna ifrån oss. Mose bad för folket.
Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
8 Då sade Herren till Mose: Gör dig en kopparorm, och res honom upp för ett tecken; hvilken som biten är, och ser uppå honom, han skall lefva.
Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
9 Så gjorde Mose en kopparorm, och reste honom upp för ett tecken, och om någor vardt biten af orme, så såg han på den kopparormen, och blef vid lif.
Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
10 Och Israels barn drogo ut, och lägrade sig i Oboth.
Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
11 Och ifrån Oboth drogo de ut, och lägrade sig i Ijim vid berget Abarim, uti den öknene tvärtöfver Moab österut.
Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
12 Dädan drogo de, och lägrade sig vid den bäcken Sared.
Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
13 Dädan drogo de, och lägrade sig på denna sidone vid Arnon, hvilket i öknene är, och sträcker sig ut ifrå de Amoreers landsändar; ty Arnon är Moabs landamäre, emellan Moab och de Amoreer.
Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
14 Deraf säger man uti den bokene om Herrans strider: Den höga bergklippan allt intill skyn, och intill Arnons bäck;
Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
15 Och intill bäcksens källo, hvilken räcker allt intill den staden Ar, och böjer sig, och är Moabs gränsa.
ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
16 Och dädan drogo de till brunnen; det är den brunnen, der Herren af sade till Mose: Församla folket, jag vill gifva dem vatten.
Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
17 Då söng Israel denna visona, och söngo emot hvarannan öfver brunnen:
Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
18 Denna är den brunnen, som de Förstar grafvit hafva; de ädle i folket hafva grafvit honom, genom läraren och deras stafrar. Ifrå denne öknene drogo de till Mattana;
chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 Och ifrå Mattana till Nahaliel, och ifrå Nahaliel till Bamoth;
Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
20 Och ifrå Bamoth till den dalen, som ligger i Moabs mark, vid det höga berget Pisga, som vet åt öknene.
ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
21 Och Israel sände båd till Sihon, de Amoreers Konung, och lät säga honom:
Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
22 Låt mig draga igenom ditt land; vi vilje intet vika in på åkrar, eller in på vingårdar; vi vilje icke heller dricka brunnvattnet; landstråtena vilje vi fara, tilldess vi komme genom dina landsändar.
“Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
23 Men Sihon tillstadde icke Israels barn gå igenom sina landsändar; utan församlade allt sitt folk, och drog emot Israel i öknena. Och som han kom till Jahza, stridde han emot Israel.
Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
24 Men Israel slog honom med svärdsegg, och tog hans land in, ifrån Arnon allt intill Jabbok, och allt intill Ammons barn; förty Ammons landsändar voro faste.
Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
25 Alltså tog Israel alla dessa städerna, och bodde i alla de Amoreers städer, i Hesbon, och alla hans döttrar.
Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
26 Ty staden Hesbon hörde Sihon Amoreers Konunge till, och han hade tillförene stridt med de Moabiters Konung, och vunnit honom af all hans land, allt intill Arnon.
Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
27 Deraf säger man i ordspråket: Kommer till Hesbon, att man bygger och upprättar den staden Sihon.
Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
28 Ty en eld är utgången af Hesbon, en låge af den staden Sihon; han hafver uppfrätit Ar de Moabiters; och de der bo i de höjder Arnon.
“Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
29 Ve dig, Moab; du Chemos folk äst förgånget. Man hafver hans söner slagit på flyktena, och fört hans döttrar fångna till Sihon, de Amoreers Konung.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 Deras härlighet är vorden omintet, ifrå Hesbon intill Dibon; hon är förstörd allt intill Nopha, hvilken räcker allt intill Medeba.
“Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
31 Så bodde Israel uti de Amoreers lande.
“Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
32 Och Mose sände ut spejare till Jaeser, och de vunno dess döttrar, och togo de Amoreer in, som deruti voro;
Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
33 Och vände om, och drogo uppåt den vägen till Basan. Då drog Og, Konungen i Basan, ut emot dem med allt sitt folk, till att strida i Edrei.
Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
34 Och Herren sade till Mose: Frukta dig intet för honom; ty jag hafver gifvit honom i dina hand med land och folk; och du skall göra med honom, såsom du med Sihon, de Amoreers Konung, gjort hafver, hvilken i Hesbon bodde.
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
35 Och de slogo honom och hans söner, och allt hans folk, tilldess att ingen var igen; och togo det landet in.
Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.

< 4 Mosebok 21 >