< 4 Mosebok 14 >

1 Då tog hela menigheten till att skria; och folket gret den nattena.
Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
2 Och all Israels barn knorrade emot Mose och Aaron, och hela menigheten sade till dem: Ack! att vi dock hade mått dött i Egypti land, eller ännu dö måtte i denna öknene.
Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
3 Hvi förer Herren oss i detta landet, att vi skole falla för svärd, och våra hustrur och barn varda till rofs? Är icke bättre, att vi drage in uti Egypten igen?
Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
4 Och den ene sade till den andra: Låt oss häfva oss upp en höfvitsman, och fara in uti Egypten igen.
Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
5 Men Mose och Aaron föllo uppå sin ansigte för hela menighetenes församling af Israels barn.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
6 Och Josua, Nuns son, och Caleb, Jephunne son, de ock landet bespejat hade, refvo sin kläder;
Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
7 Och sade till alla menighetena af Israels barn: Landet, som vi igenomvandrat hafve till att bespeja det, är ganska godt.
ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
8 Hafver Herren vilja till oss, så förer han oss väl uti det landet, och gifver oss det; hvilket ett land är, som mjölk och hannog uti flyter.
Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
9 Faller icke ifrå Herran, och frukter eder intet för detta landsens folk; ty vi vilje äta dem upp såsom bröd. Deras beskärm är gånget ifrå dem, och Herren är med oss; frukter eder intet för dem.
koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
10 Då sade hela folket, att man skulle stena dem. Så syntes Herrans härlighet på vittnesbördsens tabernakel för all Israels barn.
Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
11 Och Herren sade till Mose: Huru länge skall detta folket försmäda mig? Och huru länge vilja de icke tro på mig genom allahanda tecken, som jag ibland dem gjort hafver?
Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
12 Jag skall slå dem med pestilentie, och förgöra dem, och göra dig till ett större och mägtigare folk, än detta är.
Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
13 Men Mose sade till Herran: Så få de Egyptier det höra; ty du hafver fört detta folket med dine kraft midt ut ifrå dem;
Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
14 Och man varder sägandes till detta lands inbyggare, som hört hafva, att du, Herre, äst ibland detta folket, att du ansigte mot ansigte sedd varder, och din molnsky står öfver dem, och du, Herre, går för dem i molnstodene om dagen, och i eldstodene om nattene;
Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
15 Och du dräpte detta folket, såsom en man; så skulle Hedningarna, som sådana rop på dig hörde, tala och säga:
Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
16 Herren förmådde icke föra det folket in uti det land, som han dem svorit hade; derföre hafver han dräpit dem i öknene.
‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
17 Så låt nu Herrans kraft stor varda, såsom du talat hafver och sagt:
“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
18 Herren är långmodig, och af stora barmhertighet, och förlåter missgerning och öfverträdelse, och låter ingen vara ostraffad, utan söker fädernas missgerningar öfver barnen, intill tredje och fjerde led.
‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
19 Så var nu nådelig öfver detta folks missgerning, efter dina stora barmhertighet, såsom du ock desso folke förlåtit hafver, allt ifrån Egypten, och härtill.
Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
20 Och Herren sade: Jag hafver förlåtit dem det, såsom du sagt hafver.
Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
21 Men så visst som jag lefver, så skall all verlden varda full af Herrans härlighet;
Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
22 Ty alle de män, som hafva sett mina härlighet, och min tecken, som jag gjort hafver uti Egypten, och uti öknene, och nu tio resor försökt mig, och icke hafva lydt mine röst;
palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
23 Ingen af dem skall få se det landet, som jag deras fäder svorit hafver; och ingen skall se det, den mig försmädat hafver.
palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
24 Men min tjenare Caleb, derföre, att en annar Anda med honom är, och hafver troliga följt mig efter, honom skall jag föra in i det landet, der han inkom; och hans säd skall intaga det;
Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
25 Dertill ock de Amalekiter och Cananeer, som i dalarna bo. I morgon vänder om, och drager in uti öknena, på den vägen åt röda hafvet.
Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
26 Och Herren talade med Mose och Aaron, och sade:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
27 Huru länge skall denna onda hopen knorra emot mig? Ty jag hafver hört Israels barnas knorran, som de emot mig knorrat hafva.
“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
28 Derföre säg till dem: Så visst som jag lefver, säger Herren, skall jag göra eder såsom I för min öron sagt hafven.
Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
29 Edra kroppar skola falla i denna öknene; och alle I, som räknade ären ifrå tjugu år och derutöfver, I som emot mig knorrat hafven,
Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
30 Skolen intet komma in uti det land, der jag mina hand på upphäfvit hafver, att jag skulle låta eder deruti bo, förutan Caleb, Jephunne son, och Josua, Nuns son.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
31 Men edor barn, der I om saden, att de skulle varda till ett rof, dem vill jag föra derin, att de skola få se det land, som I förkasten.
Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
32 Men I, med edra kroppar, skolen falla i denna öken.
Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
33 Och edor barn skola varda herdar i öknene, i fyratio år, och umgälla edart horeri, intilldess edra kroppar varda åtgångne i öknene;
Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
34 Efter talet af de fyratio dagarna, i hvilkom I landet bespejaden, ju ett år för hvar dagen, att de skola umgälla edor missgerning i fyratio år; på det I skolen förnimma, hvad det är, när jag tager mina hand ifrå.
Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
35 Jag Herren hafver det sagt, det vill jag ock så göra allom dessom onda hopenom, som sig emot mig upphäfvit hafver; uti denna öken skola de åtgå, och der dö.
Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
36 Alltså dödde af Herrans plågo alle de män, som Mose sändt hade till att bespeja landet, och igenkomne voro, och hade kommit hela menighetena till att knorra deremot;
Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
37 Dermed att de gåfvo landena ett rykte, att det var ondt.
Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
38 Men Josua, Nuns son, och Caleb, Jephunne son, blefvo lefvande, af de män, som gångne voro till att bespeja landet.
Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
39 Och Mose talade dessa orden till all Israels barn; då sörjde folket svårliga;
Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
40 Och stodo om morgonen bittida upp, och drogo upp på bergshöjdena, och sade: Här äre vi, och vilje draga upp till de rum, der Herren oss af sagt hafver; ty vi hafve syndat.
Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
41 Men Mose sade: Hvi gån I så utöfver Herrans ord? Det skall icke väl bekomma eder.
Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
42 Drager icke upp; förty Herren är icke med eder; att I icke blifven slagne för edra fiendar.
Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
43 Ty de Amalekiter och Cananeer äro der för eder; och I varden fallande för svärd, derföre, att I hafven vändt eder ifrå Herranom; och Herren skall intet vara med eder.
chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
44 Men de voro förblindade till att draga upp på bergshöjdena; men Herrans förbunds ark och Mose kommo intet utu lägret.
Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
45 Så kommo de Amalekiter och Cananeer, som på bergen bodde, neder, och slogo dem, och förföljde dem allt intill Horma.
Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

< 4 Mosebok 14 >