< Mika 4 >
1 Men i yttersta dagarna skall det berget, som Herrans hus uppå står, beredt varda, högre än all berg, och upphöjdt öfver högarna; och folk skola löpa dertill.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
2 Och månge Hedningar skola gå, och säga: Kommer, låter oss gå upp till Herrans berg, och till Jacobs Guds hus, att han lärer oss sina vägar, och vi mågom vandra på hans stigar; ty af Zion skall utgå lagen, och Herrans ord af Jerusalem.
Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
3 Han skall döma ibland mycken folk, och straffa många Hedningar i fjerran land; de skola göra sin svärd till plogbillar, och sin spjut till liar. Intet folk skall upphäfva svärd emot det andra, och skola intet örlig mer föra.
Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
4 Hvar och en skall sitta under sitt vinträ och fikonaträ, utan fruktan; ty Herrans Zebaoths mun hafver det talat.
Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
5 Ty hvart och ett folk skall vandra uti sins guds namn; men vi skole vandra i Herrans vår Guds Namn, alltid och i evighet.
Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
6 På den tiden, säger Herren, vill jag församla den halta, och sammansamka den fördrefna, och den jag plågat hafver;
“Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
7 Och vill göra med den halta, att hon skall få arfvingar, och göra den svaga till stort folk. Och Herren skall vara Konung öfver dem på Zions berg, ifrå nu och i evighet.
Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
8 Och du torn Eder, ett dottrenes Zions fäste, din gyldene ros skall komma, ditt förra herradöme, dottrenes Jerusalems rike.
Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
9 Hvarföre håller du dig då intill andra vänner, lika som du icke skulle fä denna Konungen; eller lika som intet vorde af denna rådgifvarenom, efter värken är dig så uppåkommen, lika som ene i barnsnöd?
Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
10 Kära, lid dock sådana värk, och stanka, du dotter Zion, lika som en i barnsnöd: ty du måste visserliga utu staden, och bo på markene, och komma till Babel; men du skall åter dädan hulpen varda; der skall Herren förlossa dig ifrå dina fiendar.
Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
11 Ty månge Hedningar skola ju församla sig emot dig, och säga: Han är tillspillogjord; vi vilje se våra lust uppå Zion.
Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
12 Men de veta intet Herrans tankar, och märka intet hans rådslag, att han hafver hemtat dem tillhopa, såsom kärfvar uti ladona.
Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
13 Derföre statt upp, och tröska, du dotter Zion; ty jag vill göra dig jernhorn och kopparklor, och du skall sönderkrossa mycken folk; så skall jag tillspillogifva deras gods Herranom, och deras håfvor honom som råder öfver hela verldena.
“Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.