< Mika 1 >

1 Detta är Herrans ord, som skedde till Micha af Maresa, uti Jothams, Ahas och Jehiskia, Juda Konungars, tid; det han såg öfver Samarien och Jerusalem.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Hörer, all folk; märk till, du land, och hvad deruti är; ty Herren Herren hafver att tala med eder; ja, Herren utu sitt helga tempel.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Ty si, Herren skall utgå af sitt rum, och nederkomma, och gå uppå höjderna i landena;
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 Så att bergen skola smälta under honom, och dalarna skola refna; såsom vax smälter för eldenom, såsom vatten som nederåt flyta.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Allt detta för Jacobs öfverträdelses skull, och för Israels hus synders skull. Hvilken är då Jacobs öfverträdelse? Är det icke Samarien? Och hvilka äro Juda höjder? Är det icke Jerusalem?
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 Och jag vill göra Samarien till en stenhop i markene, den man lägger omkring en vingård, och skall bortsläpa dess stenar uti dalen, och bryta det neder i grund.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 Alle dess afgudar skola sönderslagne varda, och all dess vinning med eld uppbränd varda, och skall jag utöda all dess beläte; ty de äro sammankomne af skökolön, och skola åter skökolön varda.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 Der måste jag gråta öfver, och jämra mig; jag måste gå blott och naken; jag måste klaga såsom drakar, och sörja såsom strutser;
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Ty till dess plågo är intet råd, hvilken allt intill Juda kommen är, och skall räcka, allt intill mins folks port i Jerusalem.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Förkunner det ju icke i Gath: låter icke höra, att I gråten; utan går in uti sörjokammaren, och sätter eder i asko.
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Du sköne stad måste omkull med all skam; den stolte varder intet mer prålandes för ångests skull; ty grannen skall taga ifrå honom hvad han hafver.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Den ohörsamma staden hoppas, att det skall icke varda så ondt; men olyckan skall komma ifrå Herranom, och intill Jerusalems port.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Du stad Lachis, spänn trafvare före, och far dädan; ty du hafver varit dottrene Zion ett exempel till synd, och hållit Israels afguderi.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Du måste gifva fångar, sil väl som Gath. Dem stadenom Achsib skall fela förbundet med Israels Konungar.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Jag skall föra dig, o Maresa, den rätta arfvingan; och det härliga Israels rike skall varda en kula.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Låt afskära håren, och gack kullot öfver din dägeliga barn; gör dig platt kullot, såsom en örn; ty de äro fångne ifrå dig bortförde.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< Mika 1 >