< Malaki 2 >

1 Och nu, I Prester, detta budet gäller eder till.
“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
2 Om I det icke hören, eller icke läggen det uppå hjertat, så att I gifven mino Namne ärona, säger Herren Zebaoth; så skall jag sända en förbannelse ibland eder, och skall förbanna edor välsignelse; ja, förbanna skall jag dem, efter I icke villen lägga det uppå hjertat.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
3 Si, jag skall förbanna edra efterkommande, och kasta eder träcken af edro offre uti edart ansigte; och han skall låda vid eder.
“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
4 Så skolen I då förnimma, att jag sådana bud till eder sändt hafver, att detta skulle vara mitt förbund med Levi, säger Herren Zebaoth.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
5 Ty mitt förbund var med honom, till lif och frid; och jag gaf honom fruktan, så att han mig fruktade, och förskräcktes för mino Namne.
Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
6 Sanningens lag var uti hans mun, och der vardt intet ondt funnet uti hans läppar; han vandrade fridsammeliga och redeliga för mig, och omvände många ifrå synd.
Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
7 Ty Prestens läppar skola bevara lärona, att man må befråga lagen af hans mun; ty han är en Herrans Zebaoths Ängel.
“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
8 Men I ären afgångne ifrå vägenom, och hafven förargat många i lagen; och hafven brutit Levi förbund, säger Herren Zebaoth.
Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Derföre hafver jag ock gjort, att I föraktade och försmädde ären för allo folkena; efter I icke hållen mina vägar, och sen till personen i lagen.
“Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
10 Ty hafvom vi icke alle en fader? Hafver icke allt en Gud skapat oss? Hvi förakte vi då den ene den andra, och ohelgom förbundet, som med våra fäder gjordt är?
Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
11 Ty Juda är vorden en föraktare, och i Israel, och i Jerusalem sker styggelse; ty Juda ohelgar Herrans helighet, den han älskar; och bolar med ens främmandes guds dotter.
Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
12 Men Herren skall den, som så gör, utrycka utu Jacobs hydda, både mästaren och lärjungan, samt med honom, som Herranom Zebaoth spisoffer offrar.
Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
13 Yttermera gören I ock, att för Herrans altare äro icke annat än tårar, och gråt, och suckande; så att jag icke mer kan sa till spisoffret, eller någrahanda tacknämligit undfå af edra händer.
China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
14 Och så sägen I: Hvarföre? Derföre att du föraktar dina kära hustru, den Herren dig tillskickat hafver, och den din maka är, hvilko du förpligtad äst.
Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
15 Alltså gjorde icke den ene, hvilken dock var af enom storom anda. Men hvad gjorde den ene? Han sökte den säden, som af Gudi tillsagd var. Derföre ser eder före för edrom anda, och ingen förakte sina kära hustru.
Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
16 Äst du henne vred, så skilj dig ifrå henne, säger Herren Israels Gud; och gif henne en klädnad för försmädelsen, säger Herren Zebaoth. Derföre ser eder före för edrom anda, och förakter henne icke.
Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
17 I hafven rett Herran med edart tal. Så sägen I då: Hvarmed hafve vi rett honom? Dermed, att I sägen: Den der illa gör, han behagar Herranom, och han hafver lust till honom; eller, hvar är nu Gud, som straffar?
Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”

< Malaki 2 >