< 3 Mosebok 27 >
1 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tala med Israels barn, och säg till dem: Om någor gör Herranom ett besynnerligit löfte, så att han skattar sig;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
3 Så skall detta vara skattningen: en mansperson tjuguåra gammal, intill sextio år, skall du skatta på femtio silfversiklar, efter helgedomens sikel;
mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
4 En qvinnosperson på tretio siklar.
Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
5 Men ifrå fem år in till tjugu år, om det är en mansperson, skall du skatta honom på tjugu siklar; en qvinnosperson på tio siklar.
Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
6 Är det en månad gammalt, intill fem år, om det är en mansperson, skall du skatta det på fem silfversiklar; en qvinno på tre silfversiklar.
Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
7 Men är det sextioåra gammalt, och derutöfver, och är en mansperson, skall du skatta honom på femton silfversiklar; en qvinno på tio siklar.
Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
8 Om han är för fattig till sådana skattning, så skall han gå för Presten, och Presten skall skatta honom; och han skall skatta honom efter som hans hand, som löftet gjort hafver, förvärfva kan.
Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
9 Om det är af boskap, det man Herranom offra må, allt det man Herranom gifver, det är heligt.
“‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
10 Man skall icke vexla det, eller förvandlat, ett godt för ett ondt, eller ett ondt för ett godt. Om någor vexlar det, ett djur för det andra, så skola de båda vara helig.
Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
11 Är det djuret orent, det man icke bör offra Herranom, så skall man hafva det fram för Presten;
Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
12 Och Presten skall skatta det, om det är godt eller ondt. Och det skall blifva vid Prestens skattning.
ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
13 Vill någor lösa det, han skall gifva femtedelen utöfver skattningena.
Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
14 Om någor helgar sitt hus, så att det skall vara Herranom heligt, så skall Presten skatta det, om det är godt eller ondt. Och efter som Presten skattar det, så skall det blifva.
“‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
15 Men om han, som det helgat hafver, vill det lösa, skall han gifva den femte delen i silfver mer än som det skattadt är, och så skall det varda hans.
Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
16 Om någor helgar Herranom ett stycke åker af sitt arfvegods, så skall den skattad varda efter som han bär. Bär han en homer korn, så skall han gälla femtio silfversiklar.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
17 Men helgar han sin åker straxt ifrå klangåret, så skall han gälla efter hans värde.
Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
18 Hafver han helgat honom efter klangåret, så skall Presten räkna honom efter de åren, som tillbakastå intill klangåret, och derefter skatta honom desto ringare.
Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
19 Vill han, som honom helgat hafver, lösa åkren, så skall han gifva femtedelen i silfver, mer än han skattad är, och så skall han varda hans.
Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
20 Vill han icke lösan, utan säljer honom enom androm, så skall han icke mer lösa honom;
Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
21 Utan den samme åkren, när han i klangåret lös utgår, skall vara helig Herranom, såsom en förspilld åker, och skall vara Prestens arfvegods.
Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
22 Om någor helgar Herranom en åker, den han köpt hafver, och icke hans arfvegods är;
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
23 Så skall Presten räkna honom hvad han gälla kan intill klangåret, och han skall på samma dagen gifva den skattningen ut, att hon skall vara Herranom helig.
wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
24 Men på klangåret skall han komma till honom igen, som honom sålt hade, att han blifver hans arfvegods i landena.
Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
25 All skattning skall ske efter helgedomens sikel; men en sikel gör tjugu gera.
Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
26 Det förstfödda ibland boskapen, det Herranom eljest tillhörer, skall ingen helga, vare sig oxe eller får; ty det är Herrans.
“‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
27 Är något orent på boskapen, så skall man lösa det efter sitt värde, och derutöfver gifva den femte delen. Vill han icke lösa det, så må det säljas efter sitt värde.
Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
28 Man skall intet spillgifvet sälja eller lösa, det någor Herranom tillspillogifver, af allt det hans ägodelar är, vare sig menniska, boskap, eller arfåker; ty allt spillgifvet är det aldrahelgasta Herranom.
“‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
29 Man skall icke lösa någon spillgifven mennisko; utan hon skall döden dö.
“‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
30 All tionde i landet, både af landsens säd, och af frukten af trän, höra Herranom till, och skola vara helig Herranom.
“‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
31 Vill någor lösa sin tiond, han skall gifva femtedelen utöfver.
Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
32 Och all tiond af fä och får, och allt det under ris går, det är en helig tiond Herranom,
Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
33 Man skall icke fråga, om det är godt eller ondt; man skall icke heller vexlat. Om någor vexlar det, så skall både vara heligt, och icke löst varda.
Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
34 Desse äro de bud, som Herren böd Mose till Israels barn på Sinai berg.
Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.