< 3 Mosebok 22 >

1 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Säg Aaron och hans söner, att de hålla sig ifrån Israels barnas helgo, hvilket de mig helga, och icke ohelga mitt helga Namn; ty jag är Herren.
“Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
3 Säg dem nu till, och deras efterkommandom: Hvilken af edor säd går till det helga, som Israels barn helga Herranom, och orenar sig så på det, hans själ skall utrotad varda för mitt anlete; ty jag är Herren.
“Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
4 Hvilken af Aarons säd är spitelsk, eller hafver ena flöd, den skall icke äta af de helgo, tilldess han varder ren. Den som kommer vid någon oren kropp, eller den som hans säd afgår i sömnen;
“Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
5 Eller den som kommer vid en matk, den honom oren är, eller en mennisko, som honom oren är, och allt det honom orenar;
kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
6 Hvilken själ kommer vid något deraf, den är oren intill aftonen, och skall icke äta af de helgo; utan skall först bada sin kropp med vatten.
Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
7 Och när solen är nedergången, och han ren vorden är, då må han äta deraf; ty det är hans spis.
Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
8 Ett as, och hvad af vilddjur rifvet är, skolen I icke äta, att I icke skolen varda orene deruppå; ty jag är Herren.
Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
9 Derföre skola de hålla mina stadgar, att de icke skola lägga synd uppå sig, och dö deröfver, när de ohelga sig; ty jag är Herren, som dem helgar.
“‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
10 Ingen annar skall äta af de helgo, ej heller Prestens husman, ej heller någon dagakarl.
“‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
11 När Presten köper ena själ för sina penningar, den må äta deraf. Och det i hans huse födt är, det må ock äta af hans bröd.
Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
12 Om Prestens dotter varder ens främmandes hustru, skall hon icke äta af dess helgas häfoffer.
Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
13 Varder hon en enka, eller utdrifven, och hafver ingen säd, och kommer igen till sins faders hus, så skall hon äta af sins faders bröd, såsom då hon ännu piga var; men ingen främmande skall äta deraf.
Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
14 Hvilken som eljest äter af de helgo ovetandes, han skall lägga femtedelen dertill, och gifva Prestenom med de helgo;
“‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
15 På det att de icke skola ohelga Israels barnas helga, som de häfoffra Herranom;
Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
16 Att de icke skola lägga missgerning och skuld på sig, när de äta af deras helgo; ty jag är Herren, som dem helgar.
ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
17 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Säg Aaron och hans söner, och all Israels barn: Hvilken Israelit eller främling i Israel vill göra sitt offer, vare sig af löfte, eller af fri vilja, att de vilja göra Herranom ett bränneoffer, det honom skall vara tacknämligit af eder;
“Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
19 Det skall vara ett mankön, och utan vank, af fä, lambom eller getom.
ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
20 Allt det som något fel hafver, skolen I icke offra; förty det varder icke tacknämligit för eder.
Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
21 Och hvilken ett tackoffer Herranom göra vill, ett besynnerligit löfte, eller af fri vilja, af fä eller får, det skall vara utan vank, att det må varda tacknämligit. Det skall hafva ingen vank.
Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
22 Är det blindt, eller brutet, eller sargadt, eller förtvinadt, eller maslogt, eller skabbogt; så skola de icke sådant offra Herranom, och intet offer deraf gifva på Herrans altare.
Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
23 En oxe eller får, som oskickeliga eller lytta lemmar hafver, må du offra af en fri vilja; men icke varder det tacknämligit för ett löfte.
Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
24 Du skall ock icke offra Herranom något det förkramadt, eller förstött, eller förslitet, eller utskuret är; och skolen sådant icke göra i edro lande.
Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
25 Du skall ock icke offra något sådant af ens främlings hand, med edars Guds bröd; ty det doger intet, och hafver en vank; derföre varder det icke tacknämligit för eder.
Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
26 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
27 När en kalf, eller lamb, eller get födt är, så skall det vara när sine moder i sju dagar; på åttonde dagen och derefter må man offra det Herranom, så är det tacknämligit.
“Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
28 Vare sig nöt eller får, så skall man icke slagta det med sin unga på enom dag.
Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
29 När I viljen göra Herranom ett lofoffer, det för eder tacknämligit skall vara;
“Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
30 Så skolen I äta det på samma dagen, och skolen intet behålla qvart intill morgonen; ty jag är Herren.
Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
31 Derföre håller min bud, och görer dem; ty jag är Herren;
“Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
32 Att I icke ohelgen mitt helga Namn, och att jag må helgad varda ibland Israels barn; ty jag är Herren, den eder helgar;
Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
33 Den eder utur Egypti land fört hafver, att jag skulle vara edar Gud: Jag är Herren.
ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”

< 3 Mosebok 22 >