< 3 Mosebok 2 >

1 Vill en själ göra Herranom ett spisoffer, så skall det vara af semlomjöl; och skall gjuta der oljo uppå, och lägga rökelse deruppå;
“‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
2 Och bära det så till Presterna, Aarons söner. Då skall Presten taga sina hand fulla af det samma semlomjölet och oljone, samt med allt rökelset, och bränna det upp på altaret till en åminnelse. Detta är ett offer, som väl luktar för Herranom.
ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
3 Det öfver är af spisoffret, skall höra Aaron och hans söner till. Det skall vara det aldrahelgasta af Herrans offer.
Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
4 Men vill han göra ett spisoffer af det i ugn bakas, så tage kakor af semlomjöl, osyrade, beblandade med oljo, och osyrade tunnkakor, smorda med oljo.
“‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
5 Men är ditt spisoffer af något det som bakadt är i panno, så skall det vara af osyradt semlomjöl, beblandadt med oljo.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
6 Och du skall delat i stycker, och gjuta der oljo uppå; så är det ett spisoffer.
Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
7 Är ock ditt spisoffer något det på halster bakadt är, så skall du göra det af semlomjöl med oljo.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
8 Och det spisoffer, som du af sådana vill göra Herranom, det skall du bära till Presten; han skall hafva det fram till altaret;
Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
9 Och häfoffra det samma spisoffret till en åminnelse, och bränna det upp på altaret. Det är ett offer, som väl luktar för Herranom.
Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
10 Det öfver är, skall höra Aaron och hans söner till. Det skall vara det aldrahelgasta af Herrans offer.
Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
11 Allt spisoffer, som I viljen offra Herranom, skolen I göra utan surdeg; ty ingen surdeg eller hannog skall deribland uppbränd varda Herranom för offer.
“‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
12 Men till en förstling skolen I offra dem Herranom; men på intet altare skola de komma till en söt lukt.
Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
13 Allt ditt spisoffer skall du salta. Och ditt spisoffer skall aldrig vara utan dins Guds förbunds salt; ty uti allt ditt offer skall du offra salt.
Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
14 Vill du göra ett spisoffer Herranom af första frukterna, skall du torka de gröna axen vid eld, och stöta dem små, och så offra spisoffer af dina första frukter;
“‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
15 Och skall låta der oljo uppå, och lägga rökelse deruppå; så är det ett spisoffer.
Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
16 Och Presten skall taga af det stötta, och af oljone med allt rökelset, och uppbränna det till en åminnelse. Det är Herranom ett offer.
Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

< 3 Mosebok 2 >