< 3 Mosebok 17 >

1 Och Herren talade med Mose, och sade:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tala med Aaron och hans söner, och all Israels barn, och säg till dem: Detta är det Herren budit hafver:
“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
3 Hvilken af Israels hus, som i lägret, eller utanför lägret, slagtar en oxa, eller lamb, eller get;
Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
4 Och intet bär fram för dörrena af vittnesbördsens tabernakel det som Herranom för ett offer buret varder inför Herrans boning, han skall för blod brottslig vara, såsom den som blod utgjutit hafver; och sådana menniska skall utrotad varda utu sitt folk.
mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
5 Derföre skola Israels barn deras offer, som de på fria markene offra vilja, bära fram för Herran, inför dörrena af vittnesbördsens tabernakel till Presten, och der offra deras tackoffer Herranom;
Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
6 Och Presten skall stänka blodet på Herrans altare inför dörrene af vittnesbördsens tabernakel, och bränna upp det feta, Herranom till en söt lukt;
Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
7 Och ingalunda mer offra djeflomen deras offer, med hvilkom de hor bedrifva. Det skall dem vara en evig rätt i deras efterkommandom.
Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
8 Derföre skall du säga dem: Hvilken menniska af Israels huse, eller ock en främling, den ibland eder är, som gör ett offer eller bränneoffer,
“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
9 Och bär det icke inför dörrena af vittnesbördsens tabernakel, att han gör det Herranom, den skall utrotad varda utu hans folk.
popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
10 Och hvilken menniska, vare sig af Israels huse, eller en främling ibland eder, äter något blod; emot honom skall jag sätta mitt anlete, och skall utrota honom midt utu hans folk;
“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
11 Ty kroppsens lif är uti blodet, och jag hafver gifvit eder det till altaret, att edra själar skola dermed försonade varda; förty blodet är försoning för lifvet.
Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
12 Derföre hafver jag sagt Israels barnom: Ingen själ ibland eder skall äta blod, och ingen främling, som ibland eder bor.
Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
13 Och hvilken menniska, vare sig af Israels huse, eller en främling ibland eder, som tager ett djur eller fogel i jagt, det man äter, han skall utgjuta dess blod, och öfvertäcka honom med jord;
“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
14 Ty kroppsens lif är i sinom blod. Och jag hafver sagt Israels barnom: I skolen ingen kropps blod äta; ty kroppsens lif är i sinom blod. Den det äter, han skall utrotad varda.
chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
15 Och hvilken själ som äter ett as, eller det af vilddjur rifvet är, vare sig en inländsk eller utländsk, han skall två sin kläder, och bada sig med vatten, och vara oren intill aftonen, så varder han ren.
“‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
16 Om han icke tvår sin kläder, eller sig icke badar, skall han bära sina missgerning.
Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”

< 3 Mosebok 17 >