< 3 Mosebok 16 >
1 Och Herren talade med Mose, sedan de två Aarons söner döde voro, då de offrade för Herranom.
Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
2 Och Herren sade: Säg dinom broder Aaron, att han icke i alla tider ingår uti den innersta helgedomen, inom förlåten inför nådastolen, som på arkenom är, att han icke dör; ty jag vill låta se mig uti ett moln på nådastolenom;
Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
3 Utan härmed skall han gå in: Med en ung stut till syndoffer, och med en vädur till bränneoffer;
“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
4 Och skall kläda den helga linna kjortelen uppå, och hafva det linna nederklädet uppå sitt kött, och gjorda sig med ett linnet bälte, och hafva den linna hatten uppå; förty det äro de helga kläden; och skall bada sitt kött med vatten, och lägga dem uppå;
Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
5 Och skall taga utaf menighetene af Israels barnom två getabockar till syndoffer, och en vädur till bränneoffer.
Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
6 Och Aaron skall hafva fram stuten, sitt syndoffer, och försona sig och sitt hus;
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
7 Och sedan taga de två bockarna, och ställa dem fram för Herran, inför dörrena af vittnesbördsens tabernakel;
Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 Och skall kasta lott öfver de två bockarna; den ena lotten Herranom, den andra fribockenom;
Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
9 Och skall offra den bocken till ett syndoffer, på hvilken Herrans lott föll.
Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
10 Men den bocken, öfver hvilken dess frias lott föll, skall han ställa lefvande fram för Herran, att han skall försona honom, och släppa den fribocken i öknena.
Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
11 Och så skall han då hafva fram sins syndoffers stut, och försona sig och sitt hus, och skall slagta honom;
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
12 Och skall taga ena panno, full med glöd af altaret, som står för Herranom, och handena fulla med stött rökverk, och bära det inom förlåten;
Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
13 Och lägga rökverket på elden inför Herranom, så att dambet af rökverket skyler nådastolen, som är på vittnesbördet, att han icke dör;
Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
14 Och skall taga blodet af stutenom, och stänka med sitt finger upp åt nådastolen, frammantill. Sju resor skall han så stänka af blodet för nådastolenom med hans finger.
Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
15 Sedan skall han slagta bocken, folkens syndoffer, och bära af hans blod derinom förlåten, och skall göra med hans blod såsom han gjorde med stutens blod, och stänka desslikes dermed frammantill, upp åt nådastolen;
“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
16 Och skall alltså försona helgedomen af Israels barnas orenhet, och ifrå deras öfverträdelse i alla deras synder. Sammalunda skall han göra vittnesbördsens tabernakel; ty de äro orene, som omkring ligga.
Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
17 Ingen menniska skall vara inuti vittnesbördsens tabernakel, när han går derin till att försona i helgedomenom, tilldess han går ut igen; och skall alltså försona sig och sitt hus, och hela Israels menighet.
Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
18 Och när han utgår till altaret, som står för Herranom, skall han försona det; och skall taga af stutens blod, och af bockens blod, och stryka på altarens horn allt omkring;
“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
19 Och skall stänka af blodet med sitt finger sju resor deruppå, och rensa, och helga det af Israels barnas orenhet.
Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
20 Och när han fullkomnat hafver helgedomens och vittnesbördsens tabernakels och altarens försoning, skall han hafva fram den lefvande bocken;
“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
21 Och skall då Aaron lägga båda sina händer på hans hufvud, och bekänna öfver honom alla Israels barnas missgerningar, och all deras öfverträdelse i alla deras synder, och skall lägga dem på bockens hufvud, och låta honom löpa genom någon mans hjelp, som förhanden är, i öknena;
Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
22 Att bocken skall bortbära alla deras missgerningar på sig uti vildmarkena; och låta honom i öknene.
Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
23 Och Aaron skall gå in uti vittnesbördsens tabernakel, och afkläda sig de linna kläden, som han på sig klädt hade, då han gick in uti helgedomen, och skall der låta blifva dem;
“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
24 Och skall bada sitt kött med vatten på heligt rum, och kläda sin egen kläder uppå, och gå derut, och göra sitt bränneoffer och folkens bränneoffer, och försona både sig och folket;
Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
25 Och bränna upp det feta af syndoffret på altarena.
Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
26 Men den, som förde fribocken ut, skall två sin kläder, och bada sitt kött med vatten, och sedan komma igen i lägret.
“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
27 Syndoffrens stut och syndoffrens bock, hvilkas blod till försoning buret vardt in i helgedomen, skall man föra utom lägret, och uppbränna i elde, både deras hud, kött och träck.
Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
28 Och den som bränner det upp, han skall två sin kläder, och bada sitt kött med vatten, och sedan komma i lägret.
Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
29 Och skall detta vara eder en evig rätt: På tionde dagenom i sjunde månadenom skolen I späka edra kroppar, och ingen gerning göra, vare sig inländsk eller utländsk ibland eder;
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
30 Förty på den dagen sker eder försoning, så att I varden rengjorde; ifrån alla edra synder varden I rengjorde för Herranom.
chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
31 Derföre skall det vara eder den störste Sabbath, och I skolen späka edra kroppar; en evig rätt vare det.
Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
32 Men den försoningen skall en Prest göra, den man vigt hafver, och hvilkens hand man fyllt hafver till en Prest i hans faders stad; och skall kläda på sig de linna kläder, som äro de helga kläden;
Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
33 Och skall alltså försona den helga helgedomen, och vittnesbördsens tabernakel, och altaret, och Presterna, och allt folket af menighetene.
Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
34 Det skall vara eder en evig rätt, att I försonen Israels barn af alla deras synder, ena reso om året. Och Mose gjorde såsom Herren honom budit hade.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.