< Klagovisorna 4 >

1 Huru är guldet så platt förmörkradt, och det fina guldet så platt förvandladt, och helgedomens stenar ligga förströdde på alla gator?
Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
2 De ädla Zions barn, lik räknad vid guld, huru äro de nu lik räknad vid lerkärile, de en pottomakares werk äro?
Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
3 Drakarna gifva sinom ungom spenarna, och dägga dem; men mins folks dotter måste obarmhertig vara, lika som en struts i öknene.
Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
4 Spenabarnena låder för törsts skull tungan vid dess gom; de unga barn ropa efter bröd, och ingen är som dem det utskifter.
Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
5 De som tillförene åto det aldrakräseligaste, de försmäkta nu på gatomen; de som tillförene uppfödde voro i silke, de måste nu ligga i träck.
Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
6 Mins folks dotters synd är större, än Sodoms synd, den uti ett ögnablick omstört vardt, och ingen hand kom dervid.
Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
7 Hennes Nazareer voro renare än snö, och blankare än mjölk; deras färga var rödare än korall, deras anseende var som en saphir.
Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
8 Men nu är deras ansigte så förmörkradt af svarthet, att man icke känner dem på gatomen; deras hud låder intill deras ben, och äro så torre som ett trä.
Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
9 Dem dräpnom med svärd var bättre än dem som af hunger dödde, hvilke försmäkta och förgås måste för hungers skull.
Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
10 De aldrabarmhertigasta qvinnorna måste koka sin egen barn; på det de skulle hafva dem till mats, uti mins folks dotters jämmer.
Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
11 Herren hafver fullkomnat sina grymhet, han hafver utgjutit sina grymma vrede; han hafver i Zion upptändt en eld, hvilken ock hans grundval upptärt hafver.
Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
12 Konungarna på jordene hade intet trott det, eller alla menniskor på verldene, att ovännen och fienden skulle igenom Jerusalems portar kommit.
Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
13 Men det är skedt för hans Propheters synder, och för hans Presters missgerningars skull, hvilka derinne utgöto de rättfärdigas blod.
Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
14 De gingo hit och dit på gatomen, lika som blinde, och voro besölade i blod; och kunde ock ej komma vid deras kläder;
Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
15 Utan ropade till dem: Viker undan, I orene, viker, viker, kommer vid ingen ting; ty de skydde vid dem, och flydde för dem, så att man ock sade ibland Hedningarna: De blifva der icke länge.
Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
16 Derföre hafver Herrans vrede förstrött dem, och vill icke mer se uppå dem, efter de icke ärade Presterna, och icke voro barmhertige öfver de äldsta.
Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
17 Likväl gapade vår ögon efter fåfängelig hjelp, tilldess de trötte vordo, då vi vänte efter ett folk, som oss dock intet hjelpa kunde.
Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
18 Man jagade oss, så att vi icke gå torde på vårom gatom; då kom ock vår ände, våra dagar äro ute, vår ände är kommen.
Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
19 Våre förföljare voro snarare än örnar under himmelen; på bergomen hafva de förföljt oss, och i öknene vaktat efter oss.
Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
20 Herrans smorde, som vår tröst var, är fången vorden i deras kulor, då de oss förstörde, på hvilken vi tröste, att vi under hans skugga ibland Hedningarna lefva skulle.
Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
21 Ja, fröjda dig, och var glad, du dotter Edom, som bor i Uz lande; ty kalken skall ock komma öfver dig; du måste också drucken och blottad varda.
Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
22 Men din ondska hafver en ända, du dotter Zion; han skall icke mer låta bortföra dig; men dina ondsko, du dotter Edom, skall han hemsöka, och upptäcka dina synder.
Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

< Klagovisorna 4 >