< Domarboken 1 >

1 Efter Josua död frågade Israels barn Herran, och sade: Ho skall ibland oss föra örliget emot de Cananeer?
Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
2 Herren sade: Juda skall föra det; si, jag hafver gifvit landet i hans hand.
Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
3 Då sade Juda till sin broder Simeon: Drag med mig upp i min lott, och låt oss strida emot de Cananeer, så vill jag åter draga med dig i din lott. Så drog Simeon med honom.
Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
4 Då nu Juda drog ditupp, gaf Herren honom de Cananeer och Phereseer i deras händer; och de slogo i Besek tiotusend män.
Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
5 Och de funno AdoniBesek i Besek; och stridde emot honom, och slogo de Cananeer och Phereseer.
Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
6 Men AdoniBesek flydde, och de jagade efter honom, fingo honom, och höggo af honom tummarna, både af hans händer och fötter.
Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
7 Då sade AdoniBesek: Sjutio Konungar, med afhuggna tummar af deras händer och fötter, hemtade upp under mitt bord; såsom jag nu gjort hafver, så hafver Gud vedergullit mig. Och de förde honom till Jerusalem, der blef han död.
Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
8 Men Juda barn stridde emot Jerusalem, och vunno det, och slogo det med svärdsegg, och brände staden upp.
Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
9 Sedan drogo Juda barn neder, till att strida emot de Cananeer, som bodde på bergen, och söderut, och i dalarna.
Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
10 Och Juda drog emot de Cananeer, som bodde i Hebron; men Hebron het i förtiden KiriathArba; och slog Sesai, och Ahiman, och Thalmai;
Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
11 Och drog dädan emot Debirs inbyggare; men Debir het i förtiden KiriathSepher.
Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
12 Och Caleb sade: Den som KiriathSepher slår och vinner, honom vill jag gifva mina dotter Achsa till hustru.
Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
13 Då vann det Athniel, Kenas son, Calebs yngsta broders; och han gaf honom sina dotter Achsa till hustru.
Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
14 Och det begaf sig, då hon indrog, vardt henne rådet, att hon skulle bedas en åker af sin fader; och hon gaf sig ifrån åsnanom. Då sade Caleb till henne: Hvad är dig?
Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
15 Hon sade: Gif mig en välsignelse; ty du hafver gifvit mig ett söderland; gif mig ock ett, som vatten hafver. Då gaf han henne ett, som vatten hade ofvan och nedan.
Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
16 Och de Keniters barn, Mose svågers, drogo upp utu Palma staden med Juda barn uti Juda öken, som ligger sunnan för den staden Arad; och gingo till, och bodde ibland folket.
Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
17 Och Juda drog åstad med hans broder Simeon, och slogo de Cananeer i Zephat, och gåfvo honom tillspillo, och kallade staden Horma.
Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
18 Dertill vann Juda Gaza med dess tillhöring, och Askelon med dess tillhöring, och Ekron med dess tillhöring.
Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
19 Och Herren var med Juda, så att han intog berget; förty han kunde icke intaga dem som i dalarna bodde, derföre, att de hade jernvagnar.
Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
20 Och de gåfvo Caleb Hebron, såsom Mose sagt hade; och han fördref derut de tre Enaks söner.
Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
21 Men BenJamins barn fördrefvo icke de Jebuseer, som bodde i Jerusalem; utan de Jebuseer bodde när BenJamins barn i Jerusalem, allt intill denna dag.
Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
22 Sammalunda drogo ock Josephs barn upp till BethEl; och Herren var med dem.
A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
23 Och Josephs hus bespejade BethEl, det tillförene het Lus.
Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
24 Och hållarena fingo se en man gå utu staden, och sade till honom: Visa oss huru vi skole komma in i staden, så vilje vi göra barmhertighet med dig.
Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
25 Och när han hade vist dem hvar de skulle komma in, slogo de staden med svärdsegg; men den mannen och all hans slägt läto de gå.
Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
26 Då drog den samme mannen in uti de Hetheers land, och byggde en stad, och kallade honom Lus. Den heter ännu i dag så.
Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
27 Och Manasse fördref icke BethSean med dess döttrar; icke heller Thaanach med dess döttrar, och icke heller de inbyggare i Dor med dess döttrar, ej heller de inbyggare i Jibleam med dess döttrar, ej heller de inbyggare i Megiddo med dess döttrar; och de Cananeer begynte till att bo i de samma landena.
Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
28 Men då Israel kom till magt, gjorde han de Cananeer skattpligtiga, och fördref dem icke.
Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
29 Sammalunda fördref icke heller Ephraim de Cananeer, som bodde i Gaser; utan de Cananeer bodde ibland dem i Gaser.
Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
30 Sebulon fördref icke heller dem som bodde i Kitron och Nahalol; utan de Cananeer bodde ibland dem, och voro skattpligtige.
Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
31 Asser fördref icke dem som bodde i Acco; icke heller dem som bodde i Zidon, i Ahlab, i Achsib, i Helbah, i Aphik och i Rehob;
A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
32 Utan de Asseriter bodde ibland de Cananeer, som i landena bodde; ty de fördrefvo dem icke.
Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
33 Napthali fördref icke dem som bodde i BethSemes, ej heller i BethAnath; utan bodde ibland de Cananeer, som i landena bodde; men de i BethSemes och i BethAnath vordo skattpligtige.
Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
34 Men de Amoreer trängde Dans barn in på bergena, och stadde dem icke till, att de kommo neder i dalarna.
Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
35 Och de Amoreer begynte bo på de bergena Heres i Ajalon och Saalbim; dock vardt Josephs hus hand dem för svår, så att de vordo skattpligtige.
Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
36 Och de Amoreers gränsa var der man uppgår till Akrabbim, och ifrå klippone, och ifrå höjdene.
Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

< Domarboken 1 >