< Domarboken 5 >

1 Då söngo Deborah och Barak, AbiNoams son, på den samma tiden, och sade:
“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
2 Lofver Herran, att Israel är åter fri vorden, och folket hafver varit der viljogt till.
“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
3 Hörer till, I Konungar, och akter uppå, I Förstar: jag vill, Herranom vill jag sjunga, Herranom Israels Gudi vill jag spela.
“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
4 Herre, då du utdrogst ifrå Seir, och gick fram ifrån Edoms mark, då skalf jorden, himmelen dröp, och skyarna dröpo vatten.
“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
5 Bergen smulto för Herranom, Sinai för Herranom Israels Gud.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
6 I Samgars, Anaths sons, tid, i Jaels tid, voro vägarna förgångne; och de som på stigarna gå skulle, de vandrade krokota vägar.
“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
7 Det fattades, bönder fattades i Israel, tilldess jag Debora uppkom, tilldess jag uppkom en moder i Israel.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
8 Ett nytt hafver Gud utvalt, portarna hafver han bestridt; ingen sköld eller spets vardt sedd ibland fyratiotusend i Israel.
Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
9 Mitt hjerta faller till Israels regenter, hvilke friviljoge äro ibland folket.
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
10 Lofver Herran, I som riden på sköna åsninnor, I som sitten för rätta; och sjunger, I som gån på vägomen.
“Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
11 Der skyttarna ropa ibland dem som vatten hemta, der säge man om Herrans rättfärdighet, om hans bönders rättfärdighet i Israel; då drog Herrans folk neder till portarna.
Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 Upp, upp, Debora, upp, upp, och sjung ena viso; upp, Barak, och fånga dina fångare, du AbiNoams son.
Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
13 Då vordo de förlåtne rådande öfver de mägtiga; Herren vardt rådandes genom mig öfver de hjeltar.
“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Utaf Ephraim var deras rot emot Amalek; och efter dig BenJamin i ditt folk. Af Machir äro komne regenter; och af Sebulon äro regerare vordne igenom skrifpennan.
Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Isaschars Förstar voro med Debora, och Isaschar var såsom Barak i dalenom, utsänder med sitt fotfolk. Ruben höll mycket af sig, och skiljde sig ifrån oss.
Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Hvi blefst du i dinom fårahyddom, till att höra hjordarnas bräkande; och höll mycket af dig, och skiljde dig ifrån oss?
Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Gilead blef hinsidon Jordan. Och hvi bor Dan ibland skeppen? Asser satt i hafsens hamn, och blef i sina förfallna byar.
Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Men Sebulons folk vågade sina själ i döden; Naphthali desslikes på höjdene af markene.
Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
19 Konungarna kommo och stridde. Då stridde de Cananeers Konungar i Thaanach, vid det vattnet Megiddo; men de hade ingen vinning deraf.
“Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Af himmelen var stridt emot dem; stjernorna i deras lopp stridde emot Sisera.
Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Den bäcken Kison vältrade dem, den bäcken Kedumim, den bäcken Kison. Träd, min själ, på de starka.
Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Då darrade hästarnas fötter, för deras starka åsittares förfärelses skull.
Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 Förbanner den staden Meros, sade Herrans Ängel; förbanner hans borgare, att de icke kommo Herranom till hjelp; till hjelp Herranom, till de hjeltar.
Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
24 Välsignad vare ibland qvinnor Jael, Hebers den Kenitens hustru; välsignad vare hon i hyddomen ibland qvinnor.
“Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Mjölk gaf hon, då han vatten beddes, och bar smör in uti en härlig skål.
Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Hon tog naglan med sin hand, och smedshammaren i sina högra hand, och slog Sisera genom hans hufvud; sönderkrossade, och genomstack hans tinningar.
Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 Till hennes fötter krökte han sig, föll neder, och lade sig; han krökte sig, och föll neder till hennes fötter; såsom han krökte sig, så låg han förderfvad.
Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
28 Sisera moder såg genom fenstret ut, och gret igenom gallren: Hvi förtöfvar hans vagn så länge, att han icke kommer? Hvi fördröja hans vagns hjul?
“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 De visesta ibland hennes qvinnor svarade, då hon så jämmerliga qvidde:
Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 Skulle de icke finna och byta rof, hvarjom manne en ung pigo eller två till byte; och Sisera brokot stickad kläder till byte, stickad brokot kläder om halsen till byte?
‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
31 Alltså, Herre, förgånge alle dine fiender; men de som honom kär hafva, de vare såsom uppgångande solen i sine magt. Och landet hade frid i fyratio år.
“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

< Domarboken 5 >