< Domarboken 3 >

1 Desse äro de Hedningar, som Herren lät blifva, på det han skulle med dem försöka Israel, som intet visste utaf Canaans örlig;
Iyi ndi mitundu ya anthu yomwe Yehova anayisiya kuti ayese nayo Aisraeli amene sanadziwe kumenya nkhondo mu Kanaani
2 Och att Israels barnas afföda måtte veta och lära strida, de som tillförene intet visste deraf;
(Yehova anachita izi kuti Aisraeli onse aphunzire kumenya nkhondo; makamaka amene nʼkale lonse sanadziwe kumenya nkhondo.
3 Nämliga de fem Philisteers Förstar, och alla Cananeer och Zidonier, och de Heveer, som bodde på Libanons berg, allt ifrå det berget BaalHermon, tilldess man kommer till Hamath.
Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
4 De samme blefvo till att försöka Israel med dem, att man måtte förfara, om de lydde Herrans bud, som han deras fäder budit hade genom Mose.
Iwowa Yehova anawasiya kuti aziyesa nawo Aisraeli kuti aone ngati angamvere malamulo a Yehova, amene anapatsa makolo awo kudzera mwa Mose.
5 Då nu Israels barn bodde ibland de Cananeer, Hetheer, Amoreer, Phereseer, Heveer och Jebuseer,
Choncho Aisraeli anakhala pakati pa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
6 Togo de deras döttrar till hustrur, och gåfvo sina döttrar deras söner, och tjente deras gudar;
Tsono Aisraeli aja amalola ana awo aamuna ndi aakazi kuti azikwatira ndi kukwatiwa ndi anthu amitundu ina. Kenaka anayamba kupembedza milungu yawo.
7 Och gjorde illa för Herranom, och förgåto Herran deras Gud, och tjente Baalim och lundom.
Aisraeli anachita zinthu zoyipira Yehova. Iwowa anayiwala Yehova Mulungu wawo ndi kumatumikira Abaala ndi Asera.
8 Då förgrymmade sig Herrans vrede öfver Israel, och sålde dem i CusanRisathaims hand, Konungens i Mesopotamien; och så tjente Israels barn CusanRisathaim i åtta år.
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeliwo ndipo anawagulitsa kwa Kusani-Risataimu mfumu ya ku Mesopotamiya. Choncho Aisraeli anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zisanu ndi zitatu.
9 Då ropade Israels barn till Herran, och Herren uppväckte dem en frälsare, som dem frälste, Athniel, Kenas son, Calebs yngste broders.
Koma pamene Aisraeliwo analirira kwa Yehova, Iye anawawutsira mpulumutsi, Otanieli mwana wamwamuna wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe. Iyeyu ndiye anawapulumutsa.
10 Och Herrans Ande var i honom, och han vardt domare i Israel, och drog ut till strid; och Herren gaf CusanRisathaim, Konungen i Syrien, i hans hand, så att hans hand vardt honom öfvermägtig.
Mzimu wa Yehova unatsika pa iye, choncho anasanduka mtsogoleri wa Israeli. Iye anapita kukamenya nkhondo, ndipo Yehova anapereka Kusani-Risataimu mfumu ya Aaramu mʼmanja mwake. Choncho anayigonjetsa.
11 Så blef landet stilla i fyratio år; och Athniel, Kenas son, blef död.
Ndipo mʼdzikomo munakhala mtendere zaka makumi anayi. Kenaka Otanieli mwana wa Kenazi anamwalira.
12 Men Israels barn gjorde ännu mer ondt för Herranom. Då stärkte Herren Eglon, de Moabiters Konung, emot Israel, derföre att de gjorde det ondt var för Herranom;
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Tsono Yehova anapatsa mphamvu Egiloni, mfumu ya Mowabu kuti alimbane ndi Aisraeli aja popeza anachita zinthu zoyipira Yehova.
13 Och församlade till sig Ammons barn och de Amalekiter; och han drog åstad, och slog Israel, och tog in Palma staden.
Egiloniyo anamemeza Aamori ndi Aamaleki kupita kukamenyana ndi Israeli, ndipo analanda Yeriko, mzinda wa migwalangwa.
14 Och Israels barn tjente Eglon, de Moabiters Konung, i aderton år.
Aisraeli anatumikira ngati akapolo Egiloni mfumu ya Mowabu kwa zaka 18.
15 Så ropade de till Herran, och Herren uppväckte dem en frälsare, Ehud, Gera son, Jemini sons; han var ofärdig i sin högra hand. Och Israels barn sände med honom skänker till Eglon, de Moabiters Konung.
Aisraeli analiranso kwa Yehova, ndipo Iye anawawutsira mpulumutsi, Ehudi. Iyeyu anali mwana wa Gera, munthu wamanzere, wa fuko la Benjamini. Aisraeli ankatumiza msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, kudzera kwa Ehudi.
16 Och Ehud gjorde sig ett tveeggadt svärd, en aln långt, och band det under sin kläder på högra låret;
Ndipo Ehudi anapanga lupanga lakuthwa kuwiri lotalika masentimita makumi asanu, ndipo anamangirira lupangalo pa ntchafu yake ya kumanja mʼkati mwa zovala zake.
17 Och bar fram skänken till Eglon, de Moabiters Konung; och Eglon var en ganska fet man.
Iye anakapereka msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, amene anali munthu wonenepa kwambiri.
18 Och när han hade fått ifrå sig skänken, öfvergaf han folket, som hade burit skänken;
Ehudi atapereka msonkhowo, anawuza anthu amene ananyamula msonkhowo kuti azipita.
19 Och vände tillbaka igen ifrå de afgudar i Gilgal; och lät båda: Jag hafver, o Konung, något hemligit tala vid dig. Han bad gifva ljud; och de gingo alle ut, som stodo omkring honom.
Iye mwini anabwerera pamalo a miyala yozokotedwa ku Giligala ndipo anati, “Zikomo mfumu, ine ndili ndi mawu achinsinsi kuti ndikuwuzeni.” Mfumuyo inawuza onse amene amayitumikira kuti akhale chete, ndipo kenaka anawatulutsa.
20 Och Ehud kom till honom in, och han satt uti en sommarsal allena; och Ehud sade: Jag hafver Guds ord till dig; då stod han upp af sinom stol.
Kenaka Ehudi anayandikira pafupi ndi mfumuyo, ndipo iyo inakhala yokha mʼchipinda chapamwamba, mozizira bwino. Tsono Ehudi anati, “Ndili ndi mawu ochokera kwa Mulungu woti ndikuwuzeni.” Mfumuyo itadzuka pa mpando wake waufumu,
21 Men Ehud räckte ut sina venstra hand, och tog svärdet af sitt högra lår, och stötte det in uti hans buk;
Ehudi ndi dzanja lake lamanzere, anasolola lupanga pa ntchafu yake ya kumanja ndi kubaya nalo mfumuyo pa mimba.
22 Så att ock skaftet följde in med bladet, och fetman innelyckte skaftet; ty han drog intet svärdet ut af hans buk, och träcken gick af honom.
Lupanga linalowa mʼmimba pamodzi ndi chogwirira chake. Mafuta anaphimba lupangalo popeza silinatulutsidwe mʼmimbamo. Ndiponso matumbo anatuluka.
23 Men Ehud gick ut genom bakdörrena, och lät igen dörrena efter sig, och slog henne i lås.
Kenaka Ehudi anatuluka panja pa khonde, atatseka ndi kukhoma zitseko za chipinda chapamwambacho.
24 Då han nu utkommen var, gingo hans tjenare in; och som de sågo, att dörren på sommarsalen igenlyckt var, sade de: Han är tilläfventyrs gången på stol i kammaren till sommarsalen.
Ehudi atachoka, atumiki a mfumu aja anabwera, ndipo ataona kuti zitseko za chipinda chapamwamba zinali zokhoma anaganiza kuti mwina mfumu ikudzithandiza mʼkatimo.
25 När de nu så länge bidt hade, att de skämdes, ty ingen lät dem dörrena upp af salen, togo de nyckelen, och läste upp; si, då låg deras herre der död på jordene.
Iwo anadikira nthawi yayitali koma popanda chochitika. Koma ataona kuti mfumuyo sikutsekulabe zitseko za chipindacho, iwo anatenga makiyi ndi kutsekula zitsekozo, ndipo anangoona mbuye wawo atagwera pansi, ali wakufa.
26 Och Ehud undflydde, medan de fördröjde, och gick fram om afgudarna, och undkom allt intill Seirath.
Ehudi anathawa pamene iwo ankadikira. Iye anadzera ku malo a miyala yozokotedwa kuja ndi kuthawa kupita ku Seiri.
27 Och då han kom derin, blåste han i basuner på Ephraims berg, och Israels barn drogo med honom af bergena, och han framför dem;
Atafika kumeneko, anayimba lipenga ku dziko la ku mapiri la Efereimu. Iye akutsogolera, Aisraeli onse anatsika naye pamodzi kuchoka ku mapiriko.
28 Och sade till dem: Följer mig efter, ty Herren hafver gifvit edra fiendar, de Moabiter, i edra händer; och de följde honom efter, och vunno Jordans färjostad, den som drager åt Moab, och läto ingen komma deröfver.
Iye anawawuza kuti, “Nditsatireni, chifukwa Yehova wapereka Amowabu, adani anu mʼmanja mwanu.” Choncho anthuwo anamutsatira, nalanda madooko a Yorodani opita ku Mowabu. Iwo sanalole kuti wina aliyense awoloke.
29 Och slogo de Moabiter af på den tiden vid tiotusend män, alltsammans ädla och stridsamma män, så att icke en undslapp.
Nthawi imeneyo anapha Amowabu pafupifupi 10,000. Ophedwawo anali anthu amphamvu komanso odziwa kumenya nkhondo, ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anathawa.
30 Alltså vordo de Moabiter på den tiden nederlagde, under Israels barnas hand; och landet var stilla i åttatio år.
Tsiku limenelo Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Israeli, ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 80.
31 Efter honom var Samgar, Anaths son; han slog sexhundrade Philisteer med en herdastaf, och frälste ock han Israel.
Ehudi atamwalira, panabwera Samugara mwana wa Anati. Iye anapha Afilisti 600 ndi ndodo yomenyera ngʼombe. Nayenso anapulumutsa Israeli.

< Domarboken 3 >