< Domarboken 20 >

1 Så drogo Israels barn ut, och församlade sig ihop, såsom en man, ifrå Dan allt intill BerSeba, och ifrå Gileads land, intill Herran i Mizpa.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 Och gingo tillhopa utaf alla vrår, all folk af all Israels slägte i Guds menighet, fyrahundradetusend män till fot, som svärd utdrogo.
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 Men BenJamins barn fingo höra, att Israels barn voro dragne upp till Mizpa, och Israels barn sade: Säger, huru det onda tillgånget är.
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 Då svarade Leviten, qvinnones man, som dräpen var, och sade: Jag kom till Gibea i BenJamin med mine frillo, till att blifva der öfver nattena;
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 Då hofvo sig upp borgarena i Gibea emot mig, och belade mig i huset, om nattena, och ville slå mig ihjäl, och skämde min frillo, så att hon blef död.
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 Så tog jag min frillo, och styckade henne, och sände det i alla Israels arfs mark; förty de hade gjort en slem ting, och galenskap i Israel.
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 Si, nu ären I här alle Israels barn, rådens vid, hvad I skolen göra dertill.
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 Då reste sig allt folket upp, såsom en man, och sade: Ingen gånge hem i sina hyddo eller i sitt hus;
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 Utan det vilje vi nu göra emot Gibea; låt oss kasta lott;
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 Och taga tio män af hundrade, och hundrade af tusend, och tusend af tiotusend, af alla Israels slägter, att de besörja spisning för folket, att de måga komma, och göra med Gibea BenJamins, efter all deras galenskap, som de i Israel bedrifvit hafva.
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 Så församlade sig till staden alle Israels män, såsom en man, och förbundo sig.
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 Och Israels slägter sände några män till alla BenJamins slägt, och läto säga dem: Hvad är det för en ond ting, som när eder skedd är?
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 Så får oss nu ut de män, Belials barn i Gibea, att vi måge dräpa dem, och låta det onda komma ifrån Israel. Men BenJamins barn ville icke lyda sina bröders Israels barnas röst;
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 Utan församlade sig utu städerna intill Gibea, till att draga ut till strids emot Israels barn.
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 Och vordo på den dagen talde BenJamins barn utu städerna, sex och tjugu tusend män, som svärd utdrogo; förutan de borgare i Gibea, de vordo talde sjuhundrade utvalde män.
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 Och ibland allt detta folket voro sjuhundrade utvalde män, som vensterhändte voro, och kunde med slungor drabba på ett hår, så att de intet felade.
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 Men de män af Israel, förutan de af BenJamin, vordo talde fyrahundradetusend män, som svärd förde, och stridsamme män voro.
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 Israels barn stodo upp, och drogo upp till Guds hus, och frågade Gud, och sade: Ho skall draga ditupp för oss till att begynna striden emot BenJamins barn? Herren sade: Juda skall begynna.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 Alltså stodo Israels barn om morgonen upp, och lägrade sig för Gibea;
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 Och hvar och en af Israel gick ut till att strida med BenJamin, och skickade sig till att strida emot Gibea.
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 Då föllo BenJamins barn ut af Gibea, och slogo på den dagen af Israel tu och tjugu tusend män till markena.
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 Men folket Israels män förmannade sig, och redde sig till att ytterligare strida på samma platsen, der de sig i den förra dagen redt hade;
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 Och Israels barn drogo upp, och greto för Herranom allt intill aftonen, och frågade Herran, och sade: Skole vi mer falla till och strida med BenJamins barn, våra bröder? Herren sade: Drager upp till dem.
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 Och då Israels barn trädde den andra dagen till att strida emot BenJamins barn,
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 Föllo de BenJamiter utu Gibea emot dem på samma dagen, och slogo ännu till markena adertontusend män af Israels barn, som alle svärd förde.
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 Då drogo all Israels barn upp, och allt folket, och kommo till Guds hus, och greto, och blefvo der för Herranom, och fastade den dagen intill aftonen, och offrade bränneoffer och tackoffer för Herranom.
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 Och Israels barn frågade Herran, och dersammastäds var Guds förbunds ark på den tiden.
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 Och Pinehas, Eleazars son, Aarons sons, stod för honom på den tiden, och sade: Skole vi mer draga ut till att strida emot BenJamins barn, våra bröder, eller skall jag vända igen? Herren sade: Drager ditupp; i morgon skall jag gifva dem i edra händer.
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 Och Israels barn beställde ett bakhåll omkring staden Gibea;
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 Och drogo så Israels barn upp på tredje dagen till BenJamins barn; och skickade sig emot Gibea, såsom i de två gånger tillförene.
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 Då drogo BenJamins barn ut emot folket, och gåfvo sig ifrå staden, och begynte till att slå och sarga några af folket, såsom förr i de två gånger, i markene på två vägar, den ene går till BethEl, och den andre till Gibea, vid tretio män i Israel.
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 Då tänkte BenJamins barn: De äro slagne för oss såsom tillförene. Men Israels barn sade: Låt oss fly, att vi måge komma dem ifrå staden ut uppå vägarna.
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 Så reste upp alle män af Israel, hvar af sitt rum, och skickade sig i BaalThamar, och det bakhållet af Israel gaf sig upp utu sitt rum, ifrå Gaba kulo;
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 Och kommo in mot Gibea tiotusend män, utvalde af hela Israel, så att striden vardt skarp; men de visste icke, att dem ondt tillstundade.
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 Alltså slog Herren BenJamin för Israels barn, så att Israels barn på den dagen förderfvade fem och tjugu tusend och hundrade män i BenJamin, som alle svärd förde.
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 Ty då BenJamins barn sågo, att de slagne voro, gåfvo Israels män dem rum; ty de förläto sig på bakhållet, som de hade beställt invid Gibea.
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 Och bakhållet skyndade sig ock, och drogo fram till Gibea, och stormade till, och slogo den hela staden med svärdsegg.
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 Och de hade en lösen sig emellan, de män af Israel och bakhållet, till att öfverfalla dem med svärd, när röken af stadenom uppslog.
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 Då nu de män af Israel vände sig i stridene, och BenJamin begynte till att slå och försarga i Israel vid tretio män; och tänkte: De äro slagne för oss såsom i den förra stridene;
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 Så begynte slå en rök af staden rättupp. Och BenJamin vände sig tillbaka; si, då gick röken af hela stadenom upp i himmelen.
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 Och de män af Israel vände ock om; då förskräcktes de män af BenJamin; förty de sågo, att dem tillstundade ondt.
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 Och de vände sig för de män af Israel på den vägen till öknena; men striden fullföljde dem; dertill de som af städerna inkomne voro, de förderfvade dem derinne.
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 Och de kringhvärfde BenJamin, och fullföljde dem allt intill Menuah, och förtrampade dem inför Gibea österut.
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 Och föllo af BenJamin adertontusend män, som alle stridsamme män voro.
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 Då vände de sig, och flydde åt öknena till den bergklippon Rimmon; men på den samma vägen slogo de femtusend män, och följde dem efter allt intill Gideom, och slogo dem af tutusend.
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 Och så föllo på den dagen af BenJamin fem och tjugu tusend män, som svärd förde, och alle stridsamme män voro.
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 Allenast sexhundrad män vände sig, och flydde åt öknena till den bergklippon Rimmon; och blefvo i Rimmons bergklippo i fyra månader.
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 Och de män af Israel kommo igen till BenJamins barn, och slogo med svärdsegg dem i stadenom, både folk och fä, och allt det man fann; och alla de städer, som de funno, uppbrände de i eld.
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

< Domarboken 20 >