< Domarboken 12 >
1 Och de af Ephraim skriade, och gingo norrut, och sade till Jephthah: Hvi drogst du i strid emot Ammons barn, och kallade icke oss, att vi hade mått dragit med dig? Vi vilje uppbränna ditt hus med dig i elde.
Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
2 Jephthah sade till dem: Jag och mitt folk hade en stor sak med Ammons barn; och jag kallade på eder, men I hulpen mig intet utu deras händer.
Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
3 Då jag nu såg, att ingen frälsare på färde var, satte jag mina själ i mina hand, och drog åstad emot Ammons barn, och Herren gaf dem i mina hand. Hvi kommen I nu hitupp till mig, till att strida emot mig?
Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
4 Och Jephthah församlade alla män i Gilead, och stridde emot Ephraim; och de män i Gilead slogo Ephraim, derföre, att de sade: Ären I dock, I Gileaditer, ibland Ephraim och Manasse, såsom de der af Ephraim beskyddas måste?
Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
5 Och de Gileaditer togo in Jordans färjostad för Ephraim. När de nu sade: Vi äre ock de beskyddade af Ephraim, låt mig fara öfver; så sade de män af Gilead till honom: Äst du en Ephrait? När han nu svarade nej,
Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
6 Så bådo de honom säga Schibboleth; så sade han Sibboleth, och kunde icke rätt säga det ut. Så togo de honom fatt, och dråpo honom vid färjostaden åt Jordan; så att på den tiden föllo af Ephraim tu och fyratio tusend.
Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
7 Och Jephthah dömde Israel i sex år. Och Jephthah den Gileaditen blef död, och vardt begrafven i de städer i Gilead.
Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
8 Efter dessom dömde Ibzan af BethLehem Israel.
Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
9 Han hade tretio söner, och tretio döttrar gifte han ut, och tretio döttrar tog han utanefter till sina söner; och dömde Israel i sju år;
Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Och blef död, och blef begrafven i BethLehem.
Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
11 Efter dessom dömde Israel Elon, en Sebulonit, och dömde Israel i tio år;
Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
12 Och blef död, och vardt begrafven i Ajalon, uti Sebulons land.
Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
13 Efter dessom dömde Israel Abdon, Hillels son, en Pirgathonit.
Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
14 Han hade fyratio söner, och tretio sonasöner, som på sjutio åsnafålar redo. Han dömde Israel i åtta år;
Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
15 Och blef död, och vardt begrafven i Pirgathon uti Ephraims lande, på de Amalekiters berg.
Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.