< Josua 13 >

1 Då nu Josua vardt gammal, och väl till ålders, sade Herren till honom: Du äst gammal vorden, och väl till ålders, och landet är ännu mycket qvart, som intagas skall:
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 Nämliga hela landet de Philisteers och hela Gessuri,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 Ifrå Sichor, som löper framom Egypten, allt intill Ekrons landsändar norrut, hvilka de Cananeer tillräknas; fem de Philisteers herrar, nämliga de Gasiter, de Asdoditer, de Askaloniter, de Gittiter, de Ekroniter, och de Aviter.
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 Men ifrå söder är hela de Cananeers land, och Mearah de Zidoniers, allt intill Aphek, och till de Amoreers landsändar;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 Dertill de Gibliters land, och hela Libanon österut, ifrå BaalGad nedanför berget Hermon, tilldess man kommer till Hamath;
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 Alle de som på bergen bo, ifrå Libanon intill det varma vattnet, och alle Zidonier; jag skall fördrifva dem för Israels barn; kasta lott derom, till att utskifta dem emellan Israel, såsom jag hafver budit dig.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Så skift nu denna landen emellan de nio slägter till arfs, och emellan den halfva slägten Manasse.
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Ty de Rubeniter och Gaditer hafva med den andra halfva Manasse undfått deras arfvedel, som Mose dem gaf på hinsidon Jordan österut, såsom Herrans tjenare Mose dem det gifvit hafver.
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 Ifrån Aroer, som ligger på bäcksens strand vid Arnon, och ifrå den staden midt i bäcken, och all den ängden Medeba allt intill Dibon;
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 Och alla Sihons, de Amoreers Konungs, städer, som satt i Hesbon, allt intill Ammons barnas landsändar;
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 Dertill Gilead, och de landsändar vid Gessuri och Maachati, och hela berget Hermon, och hela Basan, allt intill Salcha,
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 Hela Ogs rike i Basan, den i Astaroth och Edrei satt, hvilken ännu igen var af de Resar; men Mose slog dem, och fördref dem.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 Men Israels barn fördrefvo icke dem i Gessur, och i Maachath; utan de bodde, både Gessur och Maachath, ibland Israels barn allt intill denna dag.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Men de Leviters slägte gaf han ingen arfvedel; ty Herrans Israels Guds offer är deras arfvedel, såsom han dem sagt hade.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Så gaf Mose Rubens barnas slägte, efter deras ätter;
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Så att deras landsändar voro ifrån Aroer, som ligger på bäcksens strand vid Arnon, och den staden midt i bäcken, med alla slättmarkene intill Medeba;
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hesbon och alla dess städer, som ligga på slättmarkene, Dibon, BamothBaal, och BethBaalMeon,
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 Jahza, Kedemoth, Mephaath,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 Kiriathaim, Sibma, SerethSahar uppå berget Emek,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 BethPeor, de bäcker vid Pisga, och BethJesimoth,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 Och alla de städer på slättmarkene; och hela Sihons, de Amoreers Konungs, rike, som satt i Hesbon, den Mose slog med de Förstar i Midian, Evi, Rekem, Zur, Hur och Reba, hvilke Konung Sihons höfvitsmän voro, som i landena bodde.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 Dertill Bileam, Beors son, den spåmannen, slogo Israels barn med svärd, samt med de andra dräpna.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Och landamäret till Rubens barn var Jordan. Detta är nu Rubens barnas arfvedel i deras ätter, städer och byar.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Gads barnas slägte, efter deras ätter, gaf Mose,
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Så att deras landsändar voro Jaeser, och alla de städer i Gilead, och halft Ammons barnas land, allt intill Aroer, som ligger för Rabbah;
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 Och ifrå Hesbon intill RamathMizpe och Betonim; och ifrå Mahanaim allt intill Debirs landsändar;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 Men i dalenom, BethHaram, BethNimra, Succoth och Zaphon, som qvart var af Sihons rike, Konungens i Hesbon, hvilkets gränsa var Jordan, allt intill ändan af hafvet Cinnereth, på denna sidone Jordan, österut.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Detta är nu Gads barnas arfvedel, i deras ätter, städer och byar.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Den halfva Manasse barnas slägt, efter deras ätter, gaf Mose,
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Så att deras landsändar voro ifrå Mahanaim, hela Basan; hela Ogs rike, Konungens i Basan, och alla Jairs byar, som i Basan ligga, nämliga sextio städer;
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 Och halfva Gilead, Astaroth, Edrei, Ogs rikes städer i Basan, gaf han Machirs Manasse sons barnom, det är, hälftena af Machirs barnom, efter deras ätter.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Detta är det som Mose utskifte uppå Moabs mark, hinsidon Jordan in mot Jericho, österut.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Men Levi slägte gaf Mose ingen arfvedel; ty Herren Israels Gud är deras arfvedel, såsom han dem sagt hade.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Josua 13 >