< Jona 2 >
1 Och Jona bad till Herran sin Gud, i fiskens buk;
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 Och han sade: Jag ropade till Herran i mine ångest, och han svarade mig; jag ropade utu helvetes buk, och du hörde mina röst. (Sheol )
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
3 Du kastade mig uti djupet, midt i hafvet, så att floderna kommo omkring mig; alle dine våger och böljor gingo öfver mig.
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Jag tänkte, att jag bortkastad var ifrå din ögon; men jag skall ännu få se ditt helga tempel.
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Vattnen omhvärfde mig allt intill mitt lif; djupet omgrep mig, sjövassen öfvertäckte mitt hufvud.
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Jag sönk neder till bergsgrunden, jorden hade beslutit mig med sina bommar evinnerliga; men du hafver fört mitt lif utu förderfvet, Herre min Gud.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 Då min själ öfvergaf sig, tänkte jag uppå Herran, och min bön kom till dig, uti ditt helga tempel.
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 Men de som förlåta sig uppå sina gerningar, hvilka dock intet äro, de akta intet om nådena.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Men jag vill offra med tacksägelse. Min löfte vill jag betala Herranom, att han mig hulpit hafver.
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 Och Herren sade till fisken, och han utsputade Jona in uppå landet.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.