< Job 5 >

1 Nämn mig en, hvad gäller, om du någon finner; och se dig om någorstäds efter en helig.
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Men en dåra dräper väl vreden, och en ovisan dödar nitet.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Jag såg en dåra väl rotad, och jag bannade straxt hans huse:
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Hans barn skola vara fjerran ifrå helsone, och skola varda sönderkrossade i porten, der ingen hjelpare är.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Hans säd skall den hungrige uppäta, och de väpnade skola taga henne; och hans gods skola de törstige utsupa.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Förty vedermödan går icke upp af jordene, och olyckan växer icke upp af åkrenom;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Utan menniskan varder född till olycko, såsom foglarna till att flyga.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Dock vill jag nu tala om Gud, och handla om honom;
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Som gör mägtig ting, de der icke ransakas kunna; och under, som icke räknas kunna;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Den der regn gifver på jordena, och låter vatten komma på markena;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Den der upphöjer de nedriga, och upphjelper de förtryckta.
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Han gör deras anslag, som listige äro till intet, att deras hand intet kan uträtta.
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Han begriper de visa i deras listighet, och gör de klokas råd till galenskap;
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Att de om dagen löpa i mörkrena, och famla om middagen såsom om nattena.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Och han hjelper den fattiga ifrå svärdet, och ifrå deras mun; och utu dens väldigas hand;
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Och är dens fattigas tröst, att orättfärdigheten måste hålla sin mun till.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Si, salig är den menniska, den Gud straffar; derföre förkasta icke dens Allsmägtigas tuktan.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Ty han sargar, och läker; han slår, och hans hand helar.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Utaf sex bedröfvelser frälsar han dig, och i den sjunde kommer intet ondt vid dig.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 I dyr tid frälsar han dig ifrå döden, och i stridene ifrå svärdsens hand.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Han skall skyla dig för tungones gissel, att du icke skall frukta för förderf, då det kommer.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Uti förderf och hunger skall du le, och icke frukta för vilddjuren i landena;
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Utan ditt förbund skall vara med stenom på markene; och vilddjuren i landena skola hålla frid med dig.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Och du skall förnimma, att din hydda hafver frid, och skall försörja dina boning, och icke synda;
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Och skall förnimma, att din säd skall varda mycken, och dine efterkommande såsom gräs på jordene;
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Och skall i ålderdomen komma till grafva, såsom en hvetekärfve införd varder, i rättom tid.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Si, det hafve vi ransakat, och det är så; hör dertill, och rätta dig derefter.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >