< Job 35 >
1 Och Elihu svarade, och sade:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Håller du det för rätt, att du säger: Jag är rättvisare än Gud?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Ty du säger: Ho blifver något räknad för dig? Hvad hjelper det, om jag håller mig ifrå synd?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Jag vill svara dig med ordom, och dinom vännom med dig.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Se upp till himmelen, och skåda; och se uppå skyarna, att de äro dig för höge.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Om du syndar, hvad kan du skaffa emot honom? Och om din ondska är stor, hvad kan du göra honom?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Och om du äst rättfärdig, hvad kan du gifva honom, eller hvad kan han taga af dina händer?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Ene mennisko, såsom du äst, må din ondska något göra, och ene menniskos barne din rättfärdighet.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 De samme måga ropa, när dem mycket öfvervåld sker, och ropa öfver de väldigas arm;
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 De der intet säga: Hvar är Gud, min skapare, som sånger gör om nattena;
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Den oss gör lärdare än djuren på jordene, och visare än foglarna under himmelen?
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Men de skola der ock ropa öfver de ondas högmod, och han skall intet höra dem;
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ty Gud hörer icke fåfängelighetena, och den Allsmägtige ser der intet till.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Nu säger du; Du ser honom intet; men en dom är för honom, allenast förbida honom.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Om hans vrede icke så hastigt hemsöker, och intet sköter, att der så många laster äro,
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Derföre hafver Job fåfängt öppnat sin mun; och gifver onyttig ord före med oförnuft.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”